< Yoweli 2 >

1 Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
در صهیون کرنا بنوازید و در کوه مقدس من صدا بلند کنید! تمامی ساکنان زمین بلرزندزیرا روز خداوند می‌آید و نزدیک است.۱
2 tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
روزتاریکی و ظلمت، روز ابرها و ظلمت غلیظ مثل فجر منبسط بر کوهها! امتی عظیم و قوی که مانندآن از ازل نبوده و بعد از این تا سالها و دهرهای بسیار نخواهد بود.۲
3 Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
پیش روی ایشان آتش می‌سوزاند و در عقب ایشان شعله ملتهب می‌گردد. پیش روی ایشان، زمین مثل باغ عدن ودر عقب ایشان، بیابان بایر است و نیز از ایشان احدی رهایی نمی یابد.۳
4 Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
منظر ایشان مثل منظراسبان است و مانند اسب‌سواران می‌تازند.۴
5 Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
مثل صدای ارابه‌ها بر قله کوهها جست و خیزمی کنند؛ مثل صدای شعله آتش که کاه رامی سوزاند؛ مانند امت عظیمی که برای جنگ صف بسته باشند.۵
6 Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
از حضور ایشان قوم هامی لرزند. تمامی رویها رنگ پریده می‌شود.۶
7 Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
مثل جباران می‌دوند، مثل مردان جنگی بر حصارهابرمی آیند و هر کدام به راه خود می‌آیند وطریقهای خود را تبدیل نمی کنند.۷
8 Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
بر یکدیگرازدحام نمی کنند، زیرا هرکس به راه خودمی خرامد. از میان حربه‌ها هجوم می‌آورند وصف های خود را نمی شکنند.۸
9 Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
بر شهرمی جهند، به روی حصارها می‌دوند، به خانه هابرمی آیند. مثل دزدان از پنجره‌ها داخل می شوند.۹
10 Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
از حضور ایشان زمین متزلزل وآسمانها مرتعش می‌شود؛ آفتاب و ماه سیاه می‌شوند و ستارگان نور خویش را باز می‌دارند.۱۰
11 Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
و خداوند آواز خود را پیش لشکر خویش بلند می‌کند، زیرا اردوی او بسیار عظیم است و آنکه سخن خود را بجا می‌آورد، قدیراست. زیرا روز خداوند عظیم و بی‌نهایت مهیب است و کیست که طاقت آن را داشته باشد.۱۱
12 “Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
و لکن الان خداوند می‌گوید با تمامی دل وبا روزه و گریه و ماتم بسوی من بازگشت نمایید.۱۲
13 Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
و دل خود را چاک کنید نه رخت خویش را وبه یهوه خدای خود بازگشت نمایید زیرا که اورئوف و رحیم است و دیرخشم و کثیراحسان و ازبلا پشیمان می‌شود.۱۳
14 Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
که می‌داند که شایدبرگردد و پشیمان شود و در عقب خود برکتی واگذارد، یعنی هدیه آردی و هدیه ریختنی برای یهوه خدای شما.۱۴
15 Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
در صهیون کرنا بنوازید وروزه را تعیین کرده، محفل مقدس را ندا کنید.۱۵
16 Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
قوم را جمع کنید، جماعت را تقدیس نمایید، پیران و کودکان و شیرخوارگان را فراهم آورید. داماد از حجره خود و عروس از حجله خویش بیرون آیند.۱۶
17 Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
کاهنانی که خدام خداوند هستنددر میان رواق و مذبح گریه کنند و بگویند: «ای خداوند بر قوم خویش شفقت فرما و میراث خویش را به عار مسپار، مبادا امت‌ها بر ایشان حکمرانی نمایند. چرا در میان قومها بگویند که خدای ایشان کجا است؟»۱۷
18 Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
پس خداوند برای زمین خود به غیرت خواهد آمد و بر قوم خویش شفقت خواهد نمود.۱۸
19 Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
و خداوند قوم خود را اجابت نموده، خواهدگفت: «اینک من گندم و شیره و روغن را برای شمامی فرستم تا از آنها سیر شوید و شما را بار دیگردر میان امت‌ها عار نخواهم ساخت.۱۹
20 “Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
و لشکرشمالی را از شما دور کرده، به زمین خشک ویران خواهم راند که مقدمه آن بر دریای شرقی وساقه‌اش بر دریای غربی خواهد بود و بوی بدش بلند خواهد شد و عفونتش برخواهد آمد زیراکارهای عظیم کرده است.»۲۰
21 Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
‌ای زمین مترس! وجد و شادی بنما زیرایهوه کارهای عظیم کرده است.۲۱
22 Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
‌ای بهایم صحرا مترسید زیرا که مرتع های بیابان سبز شد ودرختان میوه خود را آورد و انجیر و مو قوت خویش را دادند.۲۲
23 Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
‌ای پسران صهیون در یهوه خدای خویش وجد و شادی نمایید، زیرا که باران اولین را به اندازه‌اش به شما داده است وباران اول و آخر را در وقت برای شما بارانیده است.۲۳
24 Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
پس خرمن از گندم پر خواهد شد ومعصره‌ها از شیره و روغن لبریز خواهد گردید.۲۴
25 “Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
و سالهایی را که ملخ و لنبه و سوس و سن یعنی لشکر عظیم من که بر شما فرستاده بودم خوردندبه شما رد خواهم نمود.۲۵
26 Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
و غذای بسیارخورده، سیر خواهید شد و اسم یهوه خدای خودرا که برای شما کارهای عجیب کرده است، تسبیح خواهید خواند و قوم من تا به ابد خجل نخواهند شد.۲۶
27 Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
و خواهید دانست که من در میان اسرائیل می‌باشم و من یهوه خدای شما هستم ودیگری نیست و قوم من خجل نخواهند شد تاابدالاباد.۲۷
28 “Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
و بعد از آن روح خود را بر همه بشر خواهم ریخت و پسران و دختران شما نبوت خواهندنمود و پیران شما و جوانان شما رویاها خواهنددید.۲۸
29 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
و در آن ایام روح خود را بر غلامان وکنیزان نیز خواهم ریخت.۲۹
30 Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
و آیات را از خون وآتش و ستونهای دود در آسمان و زمین ظاهرخواهم ساخت.۳۰
31 Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
آفتاب به تاریکی و ماه به خون مبدل خواهند شد، پیش از ظهور یوم عظیم ومهیب خداوند.۳۱
32 Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.
و واقع خواهد شد هر‌که نام خداوند را بخواند نجات یابد زیرا در کوه صهیون و در اورشلیم چنانکه خداوند گفته است بقیتی خواهد بود و در میان باقی ماندگان آنانی که خداوند ایشان را خوانده است.۳۲

< Yoweli 2 >