< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
And Elius continued, and said,
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Hear me, ye wise men; hearken, ye that have knowledge.
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
For the ear tries words, and the mouth tastes meat.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Let us choose judgment to ourselves: let us know amount ourselves what is right.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
For Job has said, I am righteous: the Lord has removed my judgment.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
And he has erred in my judgment: my wound is severe without unrighteousness [of mine].
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
What man is as Job, drinking scorning like water?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
[saying], I have not sinned, nor committed ungodliness, nor had fellowship with workers of iniquity, to go with the ungodly.
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
For thou shouldest not say, There shall be no visitation of a man, whereas [there is] a visitation on him from the Lord.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Wherefore hear me, ye that are wise in heart: far be it from me to sin before the Lord, and to pervert righteousness before the almighty.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Yea, he renders to a man accordingly as each of them does, and in a man's path he will find him.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
And thinkest thou that the Lord will do wrong, or will the Almighty who made the earth wrest judgment?
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
And who is he that made [the whole world] under heaven, and all things therein?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
For if he would confine, and restrain his spirit with himself;
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
all flesh would die together, and every mortal would return to the earth, whence also he was formed.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Take heed lest he rebuke [thee]: hear this, hearken to the voice of words.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Behold then the one that hates iniquities, and that destroys the wicked, who is for ever just.
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
[He is] ungodly that says to a king, Thou art a transgressor, [that says] to princes, O most ungodly one.
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
[Such a one] as would not reverence the face of an honourable man, neither knows how to give honour to the great, so as that their persons should be respected.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
But it shall turn out vanity to them, to cry and beseech a man; for they dealt unlawfully, the poor being turned aside [from their right].
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
For he surveys the works of men, and nothing of what they do has escaped him.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Neither shall there be a place for the workers of iniquity to hide themselves.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
For he will not lay upon a man more [than right].
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
For the Lord looks down upon all men, who comprehends unsearchable things, glorious also and excellent things without number.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Who discovers their works, and will bring night about [upon them], and they shall be brought low.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
And he quite destroys the ungodly, for they are seen before him.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Because they turned aside from the law of God, and did not regard his ordinances,
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
so as to bring before him the cry of the needy; for he will hear the cry of the poor.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
And he will give quiet, and who will condemn? and he will hide his face, and who shall see him? whether [it be done] against a nation, or against a man also:
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
causing a hypocrite to be king, because of the waywardness of the people.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
For [there is] one that says to the Mighty One, I have received [blessings]; I will not take a pledge:
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
I will see apart from myself: do thou shew me if I have done unrighteousness; I will not do [so] any more.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Will he take vengeance for it on thee, whereas thou wilt put [it] far [from thee]? for thou shalt choose, and not I; and what thou knowest, speak thou.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Because the wise in heart shall say this, and a wise man listens to my word.
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
But Job has not spoken with understanding, his words are not [uttered] with knowledge.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Howbeit do thou learn, Job: no longer make answer as the foolish:
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
that we add not to our sins: for iniquity will be reckoned against us, if [we] speak many words before the Lord.

< Yobu 34 >