< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Then answered Zophar the Naamathite and saide,
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Doubtlesse my thoughts cause me to answere, and therefore I make haste.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
I haue heard the correction of my reproch: therefore the spirite of mine vnderstanding causeth me to answere.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Knowest thou not this of olde? and since God placed man vpon the earth,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
That the reioycing of the wicked is short, and that the ioy of hypocrites is but a moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Though his excellencie mount vp to the heauen, and his head reache vnto the cloudes,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
Yet shall hee perish for euer, like his dung, and they which haue seene him, shall say, Where is hee?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
He shall flee away as a dreame, and they shall not finde him, and shall passe away as a vision of the night,
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
So that the eye which had seene him, shall do so no more, and his place shall see him no more.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His children shall flatter the poore, and his hands shall restore his substance.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones are full of the sinne of his youth, and it shall lie downe with him in the dust.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
When wickednesse was sweete in his mouth, and he hid it vnder his tongue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
And fauoured it, and would not forsake it, but kept it close in his mouth,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
Then his meat in his bowels was turned: the gall of Aspes was in the middes of him.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
He hath deuoured substance, and hee shall vomit it: for God shall drawe it out of his bellie.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
He shall sucke the gall of Aspes, and the vipers tongue shall slay him.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
He shall not see the riuers, nor the floods and streames of honie and butter.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
He shall restore the labour, and shall deuoure no more: euen according to the substance shalbe his exchange, and he shall enioy it no more.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
For he hath vndone many: he hath forsaken the poore, and hath spoyled houses which he builded not.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Surely he shall feele no quietnes in his bodie, neither shall he reserue of that which he desired.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
There shall none of his meate bee left: therefore none shall hope for his goods.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
When he shalbe filled with his abundance, he shalbe in paine, and the hand of all the wicked shall assaile him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
He shall be about to fill his belly, but God shall sende vpon him his fierce wrath, and shall cause to rayne vpon him, euen vpon his meate.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
He shall flee from the yron weapons, and the bow of steele shall strike him through.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
The arrowe is drawen out, and commeth forth of the body, and shineth of his gall, so feare commeth vpon him.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
All darkenes shalbe hid in his secret places: the fire that is not blowen, shall deuoure him, and that which remaineth in his tabernacle, shalbe destroyed.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heauen shall declare his wickednes, and the earth shall rise vp against him.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The increase of his house shall go away: it shall flow away in the day of his wrath.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
This is the portion of the wicked man from God, and the heritage that he shall haue of God for his wordes.

< Yobu 20 >