< Yobu 11 >
1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Then answered Zophar the Naamathite, and said,
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
Should not the multitude of words be answered? and should a man full of talk be justified?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Should thy boastings make men hold their peace? and when thou mockest, shall no man make thee ashamed?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
For thou sayest, My doctrine is pure, and I am clean in thine eyes.
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
But Oh that God would speak, and open his lips against thee;
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
And that he would shew thee the secrets of wisdom, that is manifold in effectual working! Know therefore that God exacteth of thee less than thine iniquity deserveth.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Canst thou by searching find out God? canst thou find out the Almighty unto perfection?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
It is high as heaven; what canst thou do? deeper than Sheol; what canst thou know? (Sheol )
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
The measure thereof is longer than the earth, and broader than the sea.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
If he pass through, and shut up, and call unto judgment, then who can hinder him?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
For he knoweth vain men: he seeth iniquity also, even though he consider it not.
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
But vain man is void of understanding, yea, man is born as a wild ass’s colt.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
If thou set thine heart aright, and stretch out thine hands toward him;
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
If iniquity be in thine hand, put it far away, and let not unrighteousness dwell in thy tents;
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Surely then shalt thou lift up thy face without spot; yea, thou shalt be stedfast, and shalt not fear:
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
For thou shalt forget thy misery; thou shalt remember it as waters that are passed away:
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
And [thy] life shall be clearer than the noonday; though there be darkness, it shall be as the morning.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
And thou shalt be secure, because there is hope; yea, thou shalt search [about thee], and shalt take thy rest in safety.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
Also thou shalt lie down, and none shall make thee afraid; yea, many shall make suit unto thee.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
But the eyes of the wicked shall fail, and they shall have no way to flee, and their hope shall be the giving up of the ghost.