< Yeremiya 3 >

1 “Ngati munthu asudzula mkazi wake ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo? Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri? Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri. Komabe bwerera kwa ine,” akutero Yehova.
و می‌گوید: «اگر مرد، زن خود را طلاق دهدو او از وی جدا شده، زن مرد دیگری بشودآیا بار دیگر به آن زن رجوع خواهد نمود؟ مگرآن زمین بسیار ملوث نخواهد شد؟ لیکن خداوندمی گوید: تو با یاران بسیار زنا کردی اما نزد من رجوع نما.۱
2 “Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa.
چشمان خود را به بلندیها برافراز وببین که کدام جا است که در آن با تو همخواب نشده‌اند. برای ایشان بسر راهها مثل (زن ) عرب در بیابان نشستی و زمین را به زنا و بدرفتاری خودملوث ساختی.۲
3 Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula, ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe. Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere; ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
پس بارش‌ها بازداشته شد وباران بهاری نیامد و تو را جبین زن زانیه بوده، حیارا از خود دور کردی.۳
4 Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
آیا از این به بعد مرا صدانخواهی زد که‌ای پدر من، تو یار جوانی من بودی؟۴
5 kodi mudzandikwiyira nthawi zonse? Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’ Umu ndimo mmene umayankhulira, koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”
آیا غضب خود را تا به ابد خواهد نمود وآن را تا به آخر نگاه خواهد داشت؟ اینک این راگفتی اما اعمال بد را بجا آورده، کامیاب شدی.»۵
6 Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko.
و خداوند در ایام یوشیا پادشاه به من گفت: «آیا ملاحظه کردی که اسرائیل مرتد چه کرده است؟ چگونه به فراز هر کوه بلند و زیر هردرخت سبز رفته در آنجا زنا کرده است؟۶
7 Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi.
و بعداز آنکه همه این کارها را کرده بود من گفتم نزد من رجوع نما، اما رجوع نکرد و خواهر خائن اویهودا این را بدید.۷
8 Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo.
و من دیدم با آنکه اسرائیل مرتد زنا کرد و از همه جهات او را بیرون کردم وطلاق نامه‌ای به وی دادم لکن خواهر خائن اویهودا نترسید بلکه او نیز رفته، مرتکب زنا شد.۸
9 Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo.
وواقع شد که به‌سبب سهل انگاری او در زناکاریش زمین ملوث گردید و او با سنگها و چوبها زنانمود.۹
10 Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.
و نیز خداوند می‌گوید: با وجود این همه، خواهر خائن او یهودا نزد من با تمامی دل خود رجوع نکرد بلکه با ریاکاری.»۱۰
11 Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda.
پس خداوند مرا گفت: «اسرائیل مرتدخویشتن را از یهودای خائن عادلتر نموده است.۱۱
12 Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti, “‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale, pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
لهذا برو و این سخنان را بسوی شمال نداکرده، بگو: خداوند می‌گوید: ای اسرائیل مرتدرجوع نما! و بر تو غضب نخواهم نمود زیراخداوند می‌گوید: من روف هستم و تا به ابد خشم خود را نگاه نخواهم داشت.۱۲
13 Ungovomera kulakwa kwako kuti unawukira Yehova Mulungu wako. Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo pansi pa mtengo uliwonse wogudira, ndiponso kuti sunandimvere,’” akutero Yehova.
فقط به گناهانت اعتراف نما که بر یهوه خدای خویش عاصی شدی و راههای خود را زیر هر درخت سبز برای بیگانگان منشعب ساختی و خداوند می‌گوید که شما آواز مرا نشنیدید.۱۳
14 “Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse.
پس خداوند می‌گوید: ای پسران مرتد رجوع نمایید زیرا که من شوهرشما هستم و از شما یک نفر از شهری و دو نفر ازقبیله‌ای گرفته، شما را به صهیون خواهم آورد.۱۴
15 Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
و به شما شبانان موافق دل خود خواهم داد که شما را به معرفت و حکمت خواهند چرانید.۱۵
16 Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,” akutero Yehova.
«و خداوند می‌گوید که چون در زمین افزوده و بارور شوید در آن ایام بار دیگر تابوت عهد یهوه را به زبان نخواهند‌آورد و آن به‌خاطرایشان نخواهد آمد و آن را ذکر نخواهند کرد و آن را زیارت نخواهند نمود و بار دیگر ساخته نخواهد شد.۱۶
17 Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa.
زیرا در آن زمان اورشلیم راکرسی یهوه خواهند نامید و تمامی امت‌ها به آنجابه جهت اسم یهوه به اورشلیم جمع خواهند شدو ایشان بار دیگر پیروی سرکشی دلهای شریرخود را نخواهند نمود.۱۷
18 Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
و در آن ایام خاندان یهودا با خاندان اسرائیل راه خواهند رفت وایشان از زمین شمال به آن زمینی که نصیب پدران ایشان ساختم با هم خواهند آمد.۱۸
19 “Ine mwini ndinati, “‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga ndikukupatsani dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’ Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’ ndi kuti simudzaleka kunditsata.
و گفتم که من تو را چگونه در میان پسران قرار دهم و زمین مرغوب و میراث زیباترین امت‌ها را به تو دهم؟ پس گفتم که مرا پدر خواهی خواند و از من دیگرمرتد نخواهی شد.۱۹
20 Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake, momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,” akutero Yehova.
خداوند می‌گوید: هر آینه مثل زنی که به شوهر خود خیانت ورزد همچنین شما‌ای خاندان اسرائیل به من خیانت ورزیدید.۲۰
21 Mawu akumveka pa magomo, Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo chifukwa anatsata njira zoyipa ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
آواز گریه و تضرعات بنی‌اسرائیل از بلندیهاشنیده می‌شود زیرا که راههای خود را منحرف ساخته و یهوه خدای خود را فراموش کرده‌اند.۲۱
22 Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika; ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.” “Inde, tidzabwerera kwa Inu pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
‌ای فرزندان مرتد بازگشت نمایید و من ارتدادهای شما را شفا خواهم داد.» (ومی گویند): «اینک نزد تو می‌آییم زیرا که تو یهوه خدای ما هستی.۲۲
23 Ndithu kupembedza pa magomo komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu. Zoonadi chipulumutso cha Israeli chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
به درستی که ازدحام کوههااز تلها باطل می‌باشد. زیرا به درستی که نجات اسرائیل در یهوه خدای ما است.۲۳
24 Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu la ntchito za makolo athu, nkhosa ndi ngʼombe zawo, ana awo aamuna ndi aakazi.
و خجالت مشقت پدران ما، یعنی رمه و گله و پسران ودختران ایشان را از طفولیت ما تلف کرده است.۲۴
25 Tilekeni tigone pansi mwa manyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu, ife pamodzi ndi makolo athu kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”
در خجالت خود می‌خوابیم و رسوایی ما، ما رامی پوشاند زیرا که هم ما و هم پدران ما از طفولیت خود تا امروز به یهوه خدای خویش گناه ورزیده و آواز یهوه خدای خویش را نشنیده‌ایم.»۲۵

< Yeremiya 3 >