< Yeremiya 23 >
1 “Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova.
Maudits soient les pasteurs qui perdent et dispersent les brebis de leur pâturage!
2 Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova.
A cause de cela, voici ce que dit le Seigneur sur les pasteurs de mon peuple: Vous avez dispersé et repoussé mes brebis, et vous ne les avez pas visitées. Et moi je vous punirai de vos méchantes œuvres.
3 “Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana.
Moi-même je recueillerai les restes de mon peuple sur toute terre où je les ai bannis, et je les rétablirai en leurs pâturages, et ils croîtront et ils se multiplieront.
4 Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.
Et je susciterai pour eux des pasteurs qui les mèneront paître, et ils n'auront plus peur, et ils ne trembleront plus, dit le Seigneur.
5 Yehova akuti, “Masiku akubwera, pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka. Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.
Voilà que les jours arrivent, dit le Seigneur, où je susciterai pour David un soleil de justice, et un roi règnera, et il comprendra, et il rendra justice selon le jugement à toute la terre.
6 Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka ndipo Israeli adzakhala pamtendere. Dzina limene adzamutcha ndi ili: Yehova ndiye Chilungamo Chathu.
De son temps, Juda sera sauvé, et Israël s'abritera dans ses demeures en toute assurance. Et le nom que lui donnera le Seigneur sera Josédec, parmi les prophètes.
7 Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’
A cause de cela, voilà que les jours approchent, dit le Seigneur, où ils ne diront plus: Vive le Seigneur, qui a tiré la maison d'Israël de la terre d'Égypte!
8 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”
Mais: Vive le Seigneur, qui a rassemblé toute la race d'Israël, et l'a ramenée de la terre du nord et de toutes les contrées où il les avait bannis, et qui les a rétablis dans leur héritage!
9 Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
Parmi les prophètes, je suis celui au cœur brisé; tous mes os ont été ébranlés; je suis devenu comme un homme meurtri ou comme un homme pris de vin, à la vue du Seigneur et de la magnificence de sa gloire.
10 Dziko ladzaza ndi anthu achigololo; lili pansi pa matemberero. Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma. Aneneri akuchita zoyipa ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
Devant sa face, la terre est en deuil, et les pâturages du désert sont desséchés; et la course de ces hommes est devenue mauvaise, et leur force pareillement.
11 “Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova. Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,” akutero Yehova.
Le prêtre et le prophète se sont souillés; jusque dans mon temple j'ai vu leur corruption.
12 “Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera; adzawapirikitsira ku mdima ndipo adzagwera kumeneko. Adzaona zosaona mʼnthawi ya chilango chawo,” akutero Yehova.
A cause de cela, que leur voie soit glissante et sombre, et ils y trébucheront, et ils y tomberont; car j'amènerai sur eux des maux en l'année où je les visiterai.
13 “Pakati pa aneneri a ku Samariya ndinaona chonyansa ichi: Ankanenera mʼdzina la Baala ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
Et les prophètes de Samarie, j'ai vu en eux des iniquités; ils ont prophétisé par Baal, et ils ont égaré mon peuple d'Israël.
14 Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu ndaonapo chinthu choopsa kwambiri: amachita chigololo, amanena bodza ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa. Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake. Kwa Ine anthu onsewa ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
Et les prophètes de Jérusalem, j'ai vu en eux des choses horribles; adultères, cheminant dans le mensonge, prenant de toutes mains pour ne point détourner les méchants de leurs voies, ils ont tous été pour moi comme Sodome, et les habitants de Jérusalem comme Gomorrhe.
15 Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawadyetsa zakudya zowawa ndi kuwamwetsa madzi a ndulu, chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
A cause de cela, ainsi dit le Seigneur: Voilà que je vais les nourrir de douleurs, et je les abreuverai d'eau saumâtre, parce que des prophètes de Jérusalem est sortie la souillure de toute la terre.
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu; zomwe aloserazo nʼzachabechabe. Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi, osati zochokera kwa Yehova.
Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: N'écoutez point les discours des prophètes, parce qu'ils ont des visions vaines; ils parlent selon leur cœur, et non selon la bouche de Dieu.
17 Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti, ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti, ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’”
Ils disent à ceux qui rejettent la parole du Seigneur: La paix sera avec vous; et à ceux qui courent après leurs désirs et après les égarements de leurs cœurs: Il ne vous arrivera rien de mal.
18 Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova? Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake? Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
Car qui a assisté au conseil du Seigneur? qui a vu sa parole? qui l'a entendue de ses oreilles?
19 Taonani ukali wa Yehova uli ngati chimphepo chamkuntho, inde ngati namondwe. Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
Voilà un tremblement de terre venu du Seigneur, et sa colère produit ce tremblement; elle viendra frapper les impies.
20 Mkwiyo wa Yehova sudzaleka mpaka atachita zonse zimene anatsimikiza mu mtima mwake. Mudzazizindikira bwino zimenezi masiku akubwerawa.”
Et la colère du Seigneur ne se détournera plus qu'elle n'ait accompli toutes les résolutions de son cœur; et à la fin des jours ils comprendront.
21 Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa, komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo; Ine sindinawayankhule, komabe iwo ananenera.
Je n'ai point envoyé ces prophètes, et ils ont couru d'eux-mêmes; je ne leur ai rien dit, et d'eux-mêmes ils ont prophétisé.
22 Iwo akanakhala pa msonkhano wanga ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga. Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa kuti aleke machimo awo.”
Et s'ils avaient assisté à mon conseil, s'ils avaient entendu mes paroles, je les aurais corrigés, et corrigé mon peuple de ses mauvaises inclinations.
23 Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi, ndiye sindine Mulungu?
Je suis Dieu de près, dit le Seigneur; ne suis-je pas aussi Dieu de loin?
24 Kodi wina angathe kubisala Ine osamuona?” “Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?” Akutero Yehova.
Qui se cachera dans le secret, sans que je le découvre? Est-ce que je ne remplis pas le ciel et la terre? dit le Seigneur.
25 “Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’
J'ai entendu ce que disent les prophètes, ce qu'ils prophétisent en mon nom; ils mentent quand ils disent: J'ai eu un songe.
26 Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo.
Jusques à quand en sera-t-il ainsi du cœur de ces prophètes, qui prophétisent le mensonge, en prophétisant les séductions de leur cœur?
27 Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala.
Ils s'imaginent faire oublier ma loi par des songes que chacun se raconte, comme d'autres ont fait oublier mon nom à leurs pères à cause de Baal?
28 Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga?
Que le prophète qui a eu un songe le raconte; que celui à qui est venue ma parole annonce selon la vérité. Qu'est-ce que la paille auprès du grain? Ainsi en est-il de mes paroles, dit le Seigneur.
29 Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.
Mes paroles ne sont-elles pas comme le feu, dit le Seigneur, ou comme la hache qui fend un rocher?
30 Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.”
Voilà pourquoi je suis contre les prophètes, dit le Seigneur Dieu, qui dérobent mes paroles à leurs frères.
31 Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’”
Voilà pourquoi je suis contre les prophètes qui prophétisent de la langue et disent les rêves de leur sommeil.
32 Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.
Voilà pourquoi je suis contre les prophètes qui prophétisent d'après des songes trompeurs et les racontent, et qui ont égaré mon peuple par leurs mensonges et leurs erreurs; et je ne les avais pas envoyés, et je ne leur avais rien prescrit, et ils ne seront d'aucun secours à ce peuple.
33 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’
Et si ce peuple, ou le prêtre, ou le prophète demandent quel est le fardeau du Seigneur, dis-leur: Vous êtes ce fardeau, et je vous briserai, dit le Seigneur.
34 Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake.
Si le prophète ou quelqu'un des prêtres ou du peuple se sert de ce mot: Le fardeau du Seigneur, je punirai cet homme et sa maison.
35 Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’
Voici ce que vous direz chacun à votre ami, chacun à votre frère: Qu'a dit le Seigneur? quelle est la parole du Seigneur?
36 Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu.
Mais ne prononcez plus ce mot: Le fardeau du Seigneur; car c'est votre parole qui sera un fardeau pour lui.
37 Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’
C'est pourquoi il faut dire: Le Seigneur Dieu nous a-t-il parlé?
38 Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule,
Voici donc ce que dit le Seigneur notre Dieu: En punition de ce que vous avez prononcé ce mot: Fardeau du Seigneur, après que j'eus envoyé vers vous, et que je vous eus fait dire: Ne dites plus: Le fardeau du Seigneur;
39 ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu.
A cause de cela, voilà que moi je vous prends et vous brise, vous et cette ville, que j'ai donnée à vous et à vos pères.
40 Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’”
Et je vous marquerai d'un éternel opprobre, d'une honte éternelle qui ne sera jamais oubliée.