< Yeremiya 14 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
Слово Господнє до Єремії, що було в справі посу́хи.
2 “Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
„Упала в жало́бу Юдея, а брами її ослабі́ли, насу́пилися на землі, і знявся крик Єрусалиму.
3 Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
А вельмо́жі її своїх слуг посилають по во́ду, — вони йдуть до крини́ці — й води не знахо́дять, їхній по́суд порожній верта́ється. Засоро́мляться та зашарі́ють вони, і свої го́лови понакрива́ють.
4 Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
Тому́, що земля стала спра́гла, бо дощу́ не було на землі, засоро́милися рільники́, свої го́лови понакрива́ли.
5 Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
Навіть ла́ня на полі поро́дить сарня́тко та й кине, бо немає трави.
6 Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
Навіть дикі осли́ поставали на голих гора́х, вітер втягують, мов ті шака́ли, і ме́ркнуть їм очі, бо немає трави.
7 Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
Якщо проти нас свідчать наші провини, о Господи, то зроби ради Йме́ння Свого́, бо намно́жились наші відсту́пники, ми Тобі нагріши́ли!
8 Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
О надіє Ізраїлева, о Спасителю в ча́сі недолі, — нащо будеш Ти в Кра́ї, як той чужани́ця, й як той подоро́жній, що намета лише на ночлі́г розтяга́є?
9 Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
Нащо будеш Ти, мов людина остовпі́ла, немов той сила́ч, що не може спасти́? Таж Ти в нашій сере́дині, Господи, Йме́ння ж Твоє на нас кли́четься, — не залиша́й нас!
10 Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
Так говорить Господь до наро́ду цього́: Так люблять вони волочи́тись, а не стри́мувати своїх ніг, тому́ то не має Господь уподо́бання в них, — Він тепер їхню провину згада́є, і їхній гріх покарає!
11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
І промовив до мене Госпо́дь: Не молись за наро́д цей на добре йому́:
12 Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
Як вони будуть по́стити, Я не послухаю їхніх блага́нь, а коли принесуть цілопа́лення й дар, Я їх не прийму́, — бо Я повигу́блюю всіх їх мечем, і голодом, і морови́цею!
13 Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
А я відказав: О Господи, Боже! Ось пророки гово́рять до них: „Ви не бу́дете бачити меча́, і не буде вам голоду, правдивий бо мир в цьому місці вам дам!“
14 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
Та промовив до мене Господь: Ці пророки неправду Іме́нням Моїм пророкують: Я їх не посилав, і не наказував їм, і їм не говорив! Вони вам пророкують невірні виді́ння та ча́ри, нікче́мність й ома́ну свого се́рця.
15 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
Тому так промовляє Господь на пророків, які пророкують Іме́нням Моїм, хоч Я не посилав їх, та що кажуть вони: „Меч та голод не буде в цім кра́ї“: від меча́ та від голоду згинуть пророки такі!
16 Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
А наро́д, що таке пророку́ють йому́, розки́даний буде по вулицях Єрусалиму від голоду та від меча́, і не буде кому поховати його́, — вони й їхні жінки́, й їхні сини та їхні до́чки, і виллю на них їхнє зло!
17 “Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
І ти скажеш до них оце слово: Хай заходять удень та вночі мої очі слізьми́, і нехай не зати́хнуть, бо ді́вчина, доня народу мого́, буде побита великим нещастям, дуже болю́чим уда́ром!
18 Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
Якщо ви́йду на поле — ось побиті мече́м, й якщо ви́йду до міста — ось помлі́лі із го́лоду, і навіть пророк та священик шмигля́ють по кра́ю, якого не знають.
19 Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
Чи насправді покинув Ти Юду? Чи й Сіоном гиду́є душа Твоя? Чому вра́зив Ти нас — і немає нам ліку? Ми чекаємо миру — й немає добра, і ча́су вздоро́влення — та ось тільки жах!
20 Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
Знаємо, Господи, нашу безбожність, вину наших батькі́в, бо ми проти Тебе згріши́ли, —
21 Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
та не відкида́й нас ради Йме́ння Свого́, не безчесть трону слави Своєї, пам'ятай, не зламай заповіту Свого із нами!
22 Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.
Хіба є між марни́ми божка́ми пога́нів такі, що спуска́ють дощі? І чи небо саме дає зли́ву? Чи ж не Ти — Господь Бог наш? Тому́ то на Тебе наді́ємось ми, бо Ти це все чи́ниш!

< Yeremiya 14 >