< Yesaya 63 >

1 Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
Хто це гряде́ із Едо́му, у ша́тах черво́них із Боцри́? Хто Той пи́шний в убра́нні Своїм, що в ве́личі сили Своєї врочисто гряде́? — Це Я, що говорить у праведності, що вла́дний спаса́ти!
2 Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
Чого то червона одежа Твоя, а ша́ти Твої як у то́го, хто топче в чави́лі?
3 “Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
„Сам один Я чави́ло топта́в, і не було із наро́дів зо Мною ніко́го! І Я топта́в їх у гніві Своїм, і чави́в їх у лю́ті Своїй, — і бри́зкав їх сік на одежу Мою, і Я попля́мив всі ша́ти Свої.
4 Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
Бо день по́мсти — у серці Моїм, і надійшов рік Мого вику́плення!
5 Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
Я дививсь, але помічника́ не було́, і дивува́всь, бо підпо́ри Мені бракува́ло, та раме́но Моє Мені допомогло́, а Мій гнів — він підтри́мав Мене!
6 Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
І топтав Я наро́ди у гніві Своїм, і лама́в їх у лю́ті Своїй, і вилив на землю їхню кров“!
7 Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
Буду зга́дувати ла́ски Господні, Господні хвали́ за все те, що вчинив нам Госпо́дь, за велике добро́ те для дому Ізраїля, що вчинив Він для них у Своїм милосерді, і в ласці великій Своїй!
8 Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
І сказав: „Вони справді наро́д Мій, сини, що неправди не кажуть, “— і став Він для них за Спаси́теля.
9 Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
В усякому у́тиску їхньому тісно було́ і Йому, і Ангол обличчя Його їх спаса́в. Любов'ю Своєю й Своїм милосердям Він ви́купив їх, і їх підні́с і носив їх усі дні в давни́ну.
10 Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
Та стали вони неслухня́ними й Духа Святого Його засмути́ли, — і Він оберну́вся на во́рога їм, Він Сам воював проти них.
11 Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
Тоді то народ Його згадає дні да́вні, Мойсея: Де Той, що їх вивів із моря із па́стирем отари Своєї? Де Той, що в нього поклав Свого Духа Святого?
12 Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
Що Він по прави́ці Мойсея прова́див раме́но вели́ччя Свого́, що Він перед ними розді́лював во́ду, щоб зроби́ти Собі вічне Ім'я́?
13 amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
Що прова́див безо́днями їх, як коня́ на пустині, — і вони не спіткну́лись?
14 Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
Як схо́дить у долину худо́ба, так їх Дух Господній водив до спочи́нку, так і Ти вів наро́д Свій, щоб зроби́ти Собі славне Ім'я́!
15 Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
Поглянь із небе́с і побач із мешка́ння святині Своєї та слави Своєї: Де горли́вість Твоя та Твої могу́тні чи́ни? Де велике число милосердя Твого та ла́ски Твоєї, що су́проти ме́не затри́малися?
16 Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
Тільки Ти — наш Отець, бо Авраам нас не знає, а Ізраїль нас не пізна́є! Ти, Господи, Отець наш, від віку Ім'я́ Твоє: наш Викупи́тель!
17 Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
Нащо, Господи, Ти попусти́в, що ми блу́димо з доріг Твоїх, нащо робиш тверди́м наше серце, щоб ми не боялись Тебе? Вернися ради рабів Своїх, ради племе́н спа́дку Свого́!
18 Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
Спа́дщину займав час короткий святий Твій наро́д, — проти́вники наші святиню Твою потопта́ли!
19 Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.
Ми стали такими, немов би відві́ку Ти не панува́в був над нами, немов би не кли́калося Твоє Йме́ння над нами!

< Yesaya 63 >