< Yesaya 59 >

1 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
هان دست خداوند کوتاه نیست تانرهاند و گوش او سنگین نی تا نشنود.۱
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
لیکن خطایای شما در میان شما و خدای شماحایل شده است و گناهان شما روی او را از شماپوشانیده است تا نشنود.۲
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
زیرا که دستهای شمابه خون و انگشتهای شما به شرارت آلوده شده است. لبهای شما به دروغ تکلم می‌نماید وزبانهای شما به شرارت تنطق می‌کند.۳
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
احدی به عدالت دعوی نمی کند و هیچکس به راستی داوری نمی نماید. به بطالت توکل دارند و به دروغ تکلم می‌نمایند. به ظلم حامله شده، شرارت رامی زایند.۴
5 Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
از تخمهای افعی بچه برمی آورند وپرده عنکبوت می‌بافند. هرکه از تخمهای ایشان بخورد می‌میرد و آن چون شکسته گردد افعی بیرون می‌آید.۵
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
پرده های ایشان لباس نخواهدشد و خویشتن را از اعمال خود نخواهند پوشانیدزیرا که اعمال ایشان اعمال شرارت است و عمل ظلم در دستهای ایشان است.۶
7 Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
پایهای ایشان برای بدی دوان و به جهت ریختن خون بی‌گناهان شتابان است. افکار ایشان افکار شرارت است ودر راههای ایشان ویرانی و خرابی است.۷
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
طریق سلامتی را نمی دانند و در راههای ایشان انصاف نیست. جاده های کج برای خود ساخته‌اند و هر‌که در آنها سالک باشد سلامتی را نخواهد دانست.۸
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
بنابراین انصاف از ما دور شده است و عدالت به ما نمی رسد. انتظار نور می‌کشیم و اینک ظلمت است و منتظر روشنایی هستیم اما در تاریکی غلیظ سالک می‌باشیم.۹
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
و مثل کوران برای دیوار تلمس می‌نماییم و مانند بی‌چشمان کورانه راه می‌رویم. در وقت ظهر مثل شام لغزش می‌خوریم و در میان تندرستان مانند مردگانیم.۱۰
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
جمیع ما مثل خرسها صدا می‌کنیم و مانندفاخته‌ها ناله می‌نماییم، برای انصاف انتظارمی کشیم و نیست و برای نجات و از ما دورمی شود.۱۱
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
زیرا که خطایای ما به حضور تو بسیار شده و گناهان ما به ضد ما شهادت می‌دهد چونکه خطایای ما با ما است و گناهان خود را می‌دانیم.۱۲
13 Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
مرتد شده، خداوند را انکار نمودیم. از پیروی خدای خود انحراف ورزیدیم به ظلم و فتنه تکلم کردیم و به سخنان کذب حامله شده، از دل آنها راتنطق نمودیم.۱۳
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
و انصاف به عقب رانده شده وعدالت از ما دور ایستاده است زیرا که راستی درکوچه‌ها افتاده است و استقامت نمی تواند داخل شود.۱۴
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
و راستی مفقود شده است و هر‌که ازبدی اجتناب نماید خود را به یغما می‌سپارد. وچون خداوند این را دید در نظر او بد آمد که انصاف وجود نداشت.۱۵
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
و او دید که کسی نبود وتعجب نمود که شفاعت کننده‌ای وجود نداشت از این جهت بازوی وی برای او نجات آورد وعدالت او وی را دستگیری نمود.۱۶
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
پس عدالت را مثل زره پوشید و خود نجات را بر سر خویش نهاد. و جامه انتقام را به‌جای لباس در بر کرد وغیرت را مثل ردا پوشید.۱۷
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
بر وفق اعمال ایشان، ایشان را جزا خواهد داد. به خصمان خود حدت خشم را و به دشمنان خویش مکافات و به جزایرپاداش را خواهد رسانید.۱۸
19 Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
و از طرف مغرب ازنام یهوه و از طلوع آفتاب از جلال وی خواهندترسید زیرا که او مثل نهر سرشاری که باد خداوندآن را براند خواهد آمد.۱۹
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
و خداوند می‌گوید که نجات‌دهنده‌ای برای صهیون و برای آنانی که دریعقوب از معصیت بازگشت نمایند خواهد آمد.۲۰
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.
و خداوند می‌گوید: «اما عهد من با ایشان این است که روح من که بر تو است و کلام من که دردهان تو گذاشته‌ام از دهان تو و از دهان ذریت تو واز دهان ذریت ذریت تو دور نخواهد شد.» خداوند می‌گوید: «از الان و تا ابدالاباد.»۲۱

< Yesaya 59 >