< Yesaya 59 >

1 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
La main du Seigneur n'a-t-elle pas la force de sauver? A-t-il endurci ses oreilles pour ne pas entendre?
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
Non; mais vos péchés mettent une barrière entre vous et Dieu, et à cause de vos péchés il a détourné de vous son visage pour ne vous point faire miséricorde.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
Car vos mains sont souillées de sang, et vos doigts de péchés; vos lèvres parlent l'iniquité, et votre langue médite l'injustice.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
Nul ne dit des choses justes; il n'y a point de jugement sincère. Ils ont foi en des idoles; ils parlent vainement; et comme ils conçoivent la douleur, ils enfantent l'iniquité.
5 Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
Ils ont fait éclore des œufs d'aspic; ils filent des toiles d'araignée; et celui qui se dispose à manger de leurs œufs, après avoir cassé un œuf gâté, y trouve un basilic.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
Leur tissu ne fera jamais un manteau; ils ne se vêtiront jamais de leurs œuvres, car leurs œuvres sont des œuvres d'iniquité.
7 Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
Leurs pieds courent au mal; ils sont prompts à répandre le sang, et leurs pensées sont des pensées de meurtre. L'oppression et la misère sont dans leurs voies.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
Ils ne connaissent pas le chemin de la paix, et il n'est point de justice en leurs voies. Les sentiers où ils marchent sont tortueux, et ils ne connaissent point la paix.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
C'est pourquoi l'équité s'est éloignée d'eux, et jamais la justice ne les a maintenus. Ils attendaient la lumière, et les ténèbres leur sont venues; ils comptaient sur l'éclat du jour, et ils marchent dans la nuit.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
Ils touchent aux murailles comme des aveugles; ils vont à tâtons, comme s'ils n'avaient point d'yeux; ils tombent à midi comme à minuit; et ils gémissent comme des mourants.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
Ils marchent tous ensemble comme l'ours et comme la colombe; ils disent: Nous attendions le jugement, et il n'est point de salut, et il est bien loin de nous.
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
Notre iniquité est grande devant vous, Seigneur, et nos péchés se sont élevés contre nous; car nos iniquités sont en nous, et nous connaissons nos injustices.
13 Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
Nous avons vécu dans l'impiété et le mensonge; nous nous sommes éloignés de notre Dieu; nous avons dit des paroles injustes; nous avons désobéi; nous avons conçu et nourri dans nos cœurs des paroles d'iniquité.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
Nous nous sommes détournés du jugement, et la justice s'est tenue loin de nous; car la vérité est anéantie dans leurs voies, et ils n'y peuvent plus marcher dans le sentier de la droiture.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
Et la vérité leur a été ravie, et ils ont détourné leur esprit des choses de l'intelligence. Et le Seigneur l'a vu, et il s'est offensé de ce qu'ils n'avaient plus de justice.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
Il a vu, et il n'y avait pas un homme; il a observé, et nul n'était là pour résister; et il les a secourus de son bras, et il les a raffermis par sa miséricorde.
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
Il s'est revêtu de la justice comme d'une cuirasse; et il a posé sur sa tête une couronne de salut; et il s'est enveloppé d'un manteau de vengeance, et il a pris son armure,
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
Comme pour se préparer à répondre par l'outrage à ses ennemis.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
Et les hommes de l'Occident craindront le nom du Seigneur, et ceux de l'Orient craindront aussi son nom glorieux; car la violence du Seigneur sera comme un fleuve impétueux: elle viendra avec des transports.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
En faveur de Sion viendra le Rédempteur, et il éloignera les impiétés de Jacob.
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.
Et voici mon alliance avec eux, dit le Seigneur: Mon Esprit qui est en toi, et les paroles que j'ai mises en ta bouche, ne manqueront pas à ta bouche, ni à celle de ta postérité; car le Seigneur l'a dit, maintenant et pour tous les siècles.

< Yesaya 59 >