< Yesaya 53 >
1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Who will beleeue our report? and to whom is the arme of the Lord reueiled?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
But hee shall growe vp before him as a branche, and as a roote out of a dry grounde: he hath neither forme nor beautie: when we shall see him, there shall be no forme that wee should desire him.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
He is despised and reiected of men: he is a man full of sorowes and hath experience of infirmities: we hidde as it were our faces from him: he was despised and we esteemed him not.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
Surely hee hath borne our infirmities, and caried our sorowes: yet wee did iudge him, as plagued, and smitten of God, and humbled.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
But hee was wounded for our transgressions, hee was broken for our iniquities: the chastisement of our peace was vpon him, and with his stripes we are healed.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
All we like sheepe haue gone astraye: wee haue turned euery one to his owne way, and the Lord hath layed vpon him the iniquitie of vs all.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
Hee was oppressed and he was afflicted, yet did he not open his mouth: hee is brought as a sheepe to the slaughter, and as a sheepe before her shearer is dumme, so he openeth not his mouth.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Hee was taken out from prison, and from iudgement: and who shall declare his age? for he was cut out of the lande of the liuing: for the transgression of my people was he plagued.
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
And he made his graue with the wicked, and with the riche in his death, though hee had done no wickednesse, neither was any deceite in his mouth.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
Yet the Lord would breake him, and make him subiect to infirmities: when hee shall make his soule an offring for sinne, he shall see his seede and shall prolong his dayes, and the will of the Lord shall prosper in his hand.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
Hee shall see of the trauaile of his soule, and shall be satisfied: by his knowledge shall my righteous seruant iustifie many: for hee shall beare their iniquities.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Therefore will I giue him a portion with the great, and he shall deuide the spoyle with the strong, because hee hath powred out his soule vnto death: and he was counted with the transgressers, and he bare the sinne of many, and prayed for the trespassers.