< Yesaya 32 >

1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Denggenyo, agturayto a sililinteg ti maysa nga ari, ken agturayto dagiti prinsipe nga addaan hustisia.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
Maiyarigto ti tunggal maysa iti maysa a salaknib manipud iti angin ken maysa a pagkamangan manipud iti bagyo, kas kadagiti karayan iti namaga a disso, kas iti linong ti maysa a dakkel a bato iti natikag a daga.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Ket saanto nga agkudrep dagiti mata dagiti makakita, ken dumngegto a nalaing dagiti lapayag dagiti makangngeg.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Ti darasudos ket agpanunotto a nalaing nga addaan iti pannakaawat, ken ti atel ket nalaka ken nalawagto nga agsao.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Ti maag ket saanen a maawagan a madaydayaw, ken saanen a maawagan a natakneng ti manangallilaw.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Ta ti maag ket agsasao iti minamaag, ken agpangpangep ti pusona iti dakes ken saan a nadiosan nga ar-aramid, ken agsasao isuna iti biddut maibusor kenni Yahweh. Saanna nga ik-ikkan dagiti mabisin, saanna nga ik-ikkan iti danum dagiti mawaw.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Dakes dagiti wagas ti manangallilaw. Mangpanpanunot isuna kadagiti nadangkes a panggep tapno dadaelenna dagiti marigrigat babaen iti inuulbod, uray no ibagbaga dagiti marigrigat ti pudno.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Ngem ti tao a mararaem ket nasayaat dagiti panggepna; ket gapu kadagiti nasayaat nga aramidna, agtalinaedto ti kinaprogresona.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Bumangonkayo, dakayo a babbai a nanam-ay, ken denggenyo ti timekko; dakayo nga awan ti pakadanaganna nga annak a babbai, dumngegkayo kaniak.
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Ta kalpasan iti makatawen, mariribukankayonto, dakayo a babbai nga awan ti pakadanaganna, ta awanto iti maapityo nga ubas, saanto a dumteng ti panagaapit.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Agtigergerkayo, dakayo a babbai nga awan iti pakadanaganna; mariribukankayo, dakayo nga awan ti pakadanaganna; ussobenyo dagiti napipintas a pagan-anayyo ket aglabuskayo; agbidangkayo iti nakersang a lupot.
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
Agdung-awkayonto gapu kadagiti napipintas a taltalon, gapu kadagiti nabunga a puon ti ubas.
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Agtubonto dagiti siit ken dagiti mulmula a nasiit iti daga dagiti tattaok, uray dagiti amin a balbalay a sigud a naragsak iti siudad ti ragragsak.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Ta mabaybay-anto ti palasio, mapanawanto ti ili nga adu ti taona; ti turod ken ti pagwanawanan ket agbalinto a rukib iti agnanayon, pagragsakan dagiti atap nga asno, pagaraban dagiti arban;
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
agingga a maibukbok kadatayo ti Espiritu nga aggapu iti ngato, ken agbalin a nabunga a talon ti let-ang, ken maibilang a kabakiran ti nabunga a talon.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Kalpasanna, agnaedto ti hustisia iti let-ang; ken agtaengto ti kinalinteg iti nabunga a talon.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
Ti aramidto ti kinalinteg ket talna; ken ti pagbanagan ti kinalinteg, agnanayon a kinaulimek ken kinatalged.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
Agnaedto dagiti tattaok iti natalna a pagianan, kadagiti natalged a balbalay, ken kadagiti naulimek a paginanaan.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
Ngem uray no agtudo iti yelo ket madadael ti kabakiran, ken madadael a naan-anay ti siudad,
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
mabendisionankayonto nga agmulmula iti igid dagiti amin a waig, dakayo a mangibulbulos kadagiti baka ken asnoyo tapno agarab.

< Yesaya 32 >