< Yesaya 32 >
1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Voici un roi qui régnera dans la justice, et les princes gouverneront dans la justice.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
L'homme sera comme une cachette contre le vent, et un abri de la tempête, comme des ruisseaux d'eau dans un endroit sec, comme l'ombre d'un grand rocher dans une terre épuisée.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Les yeux de ceux qui voient ne s'obscurcissent pas, et les oreilles de ceux qui entendent écouteront.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Le cœur de l'impétueux comprendra la connaissance, et la langue des bègues sera prête à parler clairement.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
L'insensé ne sera plus appelé noble, ni le scélérat être hautement respecté.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Car l'insensé dira des folies, et son cœur commettra l'iniquité, de pratiquer le blasphème, et de proférer des erreurs contre Yahvé, pour vider l'âme de ceux qui ont faim, et de faire manquer le breuvage des assoiffés.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Les voies du scélérat sont mauvaises. Il élabore des plans méchants pour détruire les humbles par des paroles mensongères, même quand le nécessiteux parle juste.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Mais le noble conçoit des choses nobles, et il continuera dans les choses nobles.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Levez-vous, femmes qui êtes à l'aise! Entendez ma voix! Filles insouciantes, écoutez mon discours!
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Pendant des jours au-delà d'une année, vous serez troublées, femmes insouciantes; pour le millésime échouera. La récolte ne viendra pas.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Tremblez, vous les femmes qui êtes à l'aise! Soyez inquiets, bande d'insouciants! Déshabillez-vous, mettez-vous à nu, et mettez un sac sur votre taille.
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
Battez vos poitrines pour les champs agréables, pour la vigne féconde.
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Les épines et les ronces pousseront sur la terre de mon peuple; oui, sur toutes les maisons de joie de la ville joyeuse.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Car le palais sera abandonné. La ville populeuse sera déserte. La colline et la tour de guet seront pour toujours des repaires, un délice pour les ânes sauvages, un pâturage de troupeaux,
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
jusqu'à ce que l'Esprit soit répandu sur nous d'en haut, et le désert devient un champ fertile, et le champ fructueux est considéré comme une forêt.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Alors la justice habitera dans le désert; et la justice restera dans le champ fructueux.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
L'œuvre de la justice sera la paix, et l'effet de la justice, la tranquillité et la confiance pour toujours.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
Mon peuple vivra dans une demeure paisible, dans des logements sûrs, et dans des lieux de repos tranquilles,
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
bien que la grêle aplatisse la forêt, et la ville est complètement rasée.
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Heureux ceux qui sèment près de toutes les eaux! qui envoie les pieds du bœuf et de l'âne.