< Yesaya 3 >

1 Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
زیرا اینک خداوند یهوه صبایوت پایه ورکن را از اورشلیم و یهودا، یعنی تمامی پایه نان و تمامی پایه آب را دور خواهد کرد،۱
2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
وشجاعان و مردان جنگی و داوران و انبیا وفالگیران و مشایخ را،۲
3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
و سرداران پنجاهه وشریفان و مشیران و صنعت گران ماهر و ساحران حاذق را.۳
4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
و اطفال را بر ایشان حاکم خواهم ساخت و کودکان بر ایشان حکمرانی خواهندنمود.۴
5 Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
و قوم مظلوم خواهند شد، هرکس ازدست دیگری و هرشخص از همسایه خویش. واطفال بر پیران و پستان بر شریفان تمرد خواهندنمود.۵
6 Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
چون شخصی به برادر خویش در خانه پدرش متمسک شده، بگوید: «تو را رخوت هست پس حاکم ما شو و این خرابی در زیر دست تو باشد»،۶
7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
در آن روز او آواز خود را بلند کرده، خواهد گفت: «من علاج کننده نتوانم شد زیرا درخانه من نه نان و نه لباس است پس مرا حاکم قوم مسازید.»۷
8 Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
زیرا اورشلیم خراب شده و یهودامنهدم گشته است، از آن جهت که لسان و افعال ایشان به ضد خداوند می‌باشد تا چشمان جلال اورا به ننگ‌آورند.۸
9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
سیمای رویهای ایشان به ضدایشان شاهد است و مثل سدوم گناهان خود رافاش کرده، آنها را مخفی نمی دارند. وای برجانهای ایشان زیرا که به جهت خویشتن شرارت را بعمل آورده‌اند.۹
10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
عادلان را بگویید که ایشان را سعادتمندی خواهد بود زیرا از ثمره اعمال خویش خواهند خورد.۱۰
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
وای بر شریران که ایشان را بدی خواهد بود چونکه مکافات دست ایشان به ایشان کرده خواهد شد.۱۱
12 Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
و اما قوم من، کودکان بر ایشان ظلم می‌کنند و زنان بر ایشان حکمرانی می‌نمایند. ای قوم من، راهنمایان شماگمراه کنندگانند و طریق راههای شما را خراب می‌کنند.۱۲
13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
خداوند برای محاجه برخاسته و به جهت داوری قومها ایستاده است.۱۳
14 Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
خداوند بامشایخ قوم خود و سروران ایشان به محاکمه درخواهد آمد، زیرا شما هستید که تاکستانها راخورده‌اید و غارت فقیران در خانه های شمااست.۱۴
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
خداوند یهوه صبایوت می‌گوید: «شمارا چه شده است که قوم مرا می‌کوبید و رویهای فقیران را خرد می‌نمایید؟»۱۵
16 Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
و خداوند می‌گوید: «از این جهت که دختران صهیون متکبرند و با گردن افراشته وغمزات چشم راه می‌روند و به ناز می‌خرامند و به پایهای خویش خلخالها را به صدا می‌آورند.»۱۶
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
بنابراین خداوند فرق سر دختران صهیون را کل خواهد ساخت و خداوند عورت ایشان را برهنه خواهد نمود.۱۷
18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
و در آن روز خداوند زینت خلخالها و پیشانی بندها و هلالها را دور خواهدکرد.۱۸
19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
و گوشواره‌ها و دستبندها و روبندها را،۱۹
20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
و دستارها و زنجیرها و کمربندها و عطردانها وتعویذها را،۲۰
21 mphete ndi zipini,
و انگشترها و حلقه های بینی را،۲۱
22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
و رخوت نفیسه و رداها و شالها و کیسه‌ها را،۲۲
23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
و آینه‌ها و کتان نازک و عمامه‌ها و برقع‌ها را.۲۳
24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
و واقع می‌شود که به عوض عطریات، عفونت خواهد شد و به عوض کمربند، ریسمان و به عوض مویهای بافته، کلی و به عوض سینه بند، زنار پلاس و به عوض زیبایی، سوختگی خواهدبود.۲۴
25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
مردانت به شمشیر و شجاعانت در جنگ خواهند افتاد.۲۵
26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.
و دروازه های وی ناله و ماتم خواهند کرد، و او خراب شده، بر زمین خواهدنشست.۲۶

< Yesaya 3 >