< Yesaya 24 >
1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Ось Господь нищить землю й пусто́шить її, й оберта́є поверхню її, а мешканців її розпоро́шує.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
І стане священик як і наро́д, а пан — немов раб, пані, — як невільниця її, продаве́ць — немов той покупе́ць, боргува́льник — немов винува́тець, віри́тель — як довжни́к.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Земля буде доще́нту зруйно́вана та пограбо́вана вся, бо це слово Госпо́дь проказа́в, —
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
засумує, зів'я́не земля, ослабіє й зів'яне вселе́нна, ослабіють вельможі наро́ду землі.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
Й оскверни́лась земля під своїми мешка́нцями, бо переступи́ли зако́ни, постано́ву порушили, зламали вони запові́та відві́чного.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
Тому землю прокля́ття поїло, й оде́ржали кару мешка́нці її, тому то згоріли мешка́нці землі, і небагато людей позоста́лося.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Сумує вино молоде, виногра́дина в'я́не, усі радісносе́рді зідха́ють,
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
спини́лися радощі бубнів, галас веселуні́в переста́в, затихла потіха від гу́сел!
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
При пісні вина вже не п'ють, став гірки́м п'янкий на́пій для тих, хто його попиває.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
Зруйно́ване місто спусто́шене, всі доми́ позами́кані, щоб не ввійти.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
На вулицях крик за вином, усяка радість поме́ркла, веселість землі на вигна́ння пішла, —
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
позоста́лося в місті спусто́шення, і розбита на зва́лище брама.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
Бо так буде посеред землі, посеред наро́дів, як при оббива́нні оливки, немов при визби́руванні, коли збір винограду скінчи́вся.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
Свій голос піді́ймуть і будуть радіти, через величність Господню викри́кувати голосно будуть від моря.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
Тому Господа славте на сході, на морськи́х острова́х Ім'я Господа, Бога Ізраїлевого!
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
Ми чуємо співи від кра́ю землі: „Слава Праведному!“Але я сказав: Гину, гину, ой горе мені: Грабі́жники гра́блять, і грабую́чи, граблять грабі́жно!
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
Страх і яма та па́стка на тебе, мешка́нче землі!
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
І станеться, той, хто втікатиме від крику жа́ху, до ями впаде́, хто ж із ями вихо́дить, буде схо́плений в па́стку, бо відкриті розтво́ри згори́, а підста́ви землі затремтіли.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
Земля поруйно́вана зо́всім, земля поторо́щена, вся земля захита́лась.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
Захиталась земля, немов п'я́ний, і ру́хається, мов нічлі́жний курінь, і вчинився над нею тяжки́м її гріх, і впала вона, й більш не встане!
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
І станеться в день той, Господь навісти́ть військо висоти на висоті, і зе́мних царів на землі, —
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
і будуть зібрані ра́зом, мов в'я́зні до ями, й у в'язни́цю вони будуть за́мкнені, а по днях багатьох будуть наві́щені!
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Місяць тоді засоро́миться та застида́ється сонце, бо Господь Саваот зацарюва́в на Сіонській горі та в Єрусалимі, а перед старі́шими слава Його!