< Ahebri 6 >
1 Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu,
Bhai kwa nneyo, tushoshe kumajiganyo ga kundandubho ga a Kilishitu, tujende mmujo nkwiijiganya ga ngulupai jetu tukamilishe, tunabhujile kabhili mmajiganyo ga kundandubho, ga leka yangali ya mmbone nikwaakulupalila a Nnungu,
2 za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios )
nkali majiganyo ga namuna ya ubhatisho, na ga bhishila bhandu makono, na ga yuka bhawilenje, na ga ukumu ja pitipiti. (aiōnios )
3 Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.
A Nnungu bhapingaga, genego shitutende.
4 Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera.
Pabha bhandunji bhalangashiywenje nipaya shukilo sha kunnungu, nilundana naka Mbumu jwa Ukonjelo,
5 Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn )
nipaya kunong'a kwa lilobhe lya a Nnungu, na mashili ga shilambolyo shikwiya, (aiōn )
6 Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.
kungai niileka ngulupai yabhonji, ikakomboleka kwaatendanga bhaipetanje kabhili. Bhatendanga nneyo, ni mbuti bhanakwaakomelanga munshalabha kabhili Bhanabhabho a Nnungu, na kwaatokomaya pa bhandu.
7 Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa.
Litaka linyelwa ula papagwinji nimeya yalya, ni pwaida ja bhaalima na lyene litakalyo linapegwa mboka na a Nnungu.
8 Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.
Ikabheje limeyaga mibha na likonde likapwaa, lyene litakalyo pulibha tome na loshwa na mpelo gwakwe kujokwa moto.
9 Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso.
Ikabheje ashaambwiga ajangunji, nkali tuubheleketa nneii, twangali lipamba kwenu mmanganyanji, tumumanyi kuti nnikaguyanga itendi ili ya mmbone nkatapulwanjeje.
10 Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano.
Pabha a Nnungu ni bha aki, bhenebho bhakalibhala liengo linkutendanga na kupinga kwenunji kunnanguyenje kwa lina lyabho pabha nnakwaajangutilanga bhandunji bha ukonjelo na launo nnakwaajangutilanga.
11 Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera.
Na uwe putupinga kila mundu atumbile nneyo peyo mpaka kumpelo, nkupinga yene inkukulupalilangayo imalile.
12 Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.
Bhai nnakolanje ukata, ikabhe mmanganje malinga bhene bhaakulupalilanga nikuikakatimila, niilishi miadi ja a Nnungu.
13 Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti,
Pabha a Nnungu pubhaapele a Bhulaimu miadi, bhashinkulumbila kwa lina lyabho bhayene, pabha jwakwa ali nkulungwa kupunda a Nnungu jwa kunnumbila,
14 “Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
bhalinkuti, “Kweli shinimpe mboka na lubheleko lwalugwinji.”
15 Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.
A Bhulaimu bhakalindilileje kwa kuikakatimila nigubhapatile miadi ja a Nnungu jila.
16 Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse.
Pabha bhandunji pubhaalumbilanga bhanakwaalugulanga bhali bhakulungwa kupunda ashaayenenji, nkukong'ondela gabheleketwe kupinga peya mitau.
17 Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro.
Na bhalabho a Nnungu pabha bhashinkupinga kulangula kubhandu ga miadi jabho, kuti bhakatendebhuka mmalobhe gabho, gubhakong'ondele kwa lumbila.
18 Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira.
Bhai ipali indu ibhili, miadi na lumbila, ikakomboleka tendebhuka pabha a Nnungu bhakaabheleketa unami. Kwa nneyo uwe twaabhutushile, tunatagwa ntima tupunde kamulila ngulupai itubhishilwe.
19 Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga.
Jene ngulupaiji jinakutupa mashili malinga nanga shijikuti kuujimika ntumbwi. Jene ngulupaiji jinapelenganya lukungushi lwa pa nnango mpaka pa ukonjelo kaje.
20 Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn )
A Yeshu bhayene bhashilongolela jinjila mwenemo kwa ligongo lyetu na bhaashibha, Bhakulungwa Bhaabhishila pitipiti, malinga shibhaaliji a Melikishedeki. (aiōn )