< Genesis 17 >

1 Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
و چون ابرام نود و نه ساله بود، خداوندبر ابرام ظاهر شده، گفت: «من هستم خدای قادر مطلق، پیش روی من بخرام و کامل شو،۱
2 Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
و عهد خویش را در میان خود و تو خواهم بست، و تو را بسیاربسیار کثیر خواهم گردانید.»۲
3 Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
آنگاه ابرام به روی در‌افتاد و خدا به وی خطاب کرده، گفت:۳
4 “Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
«اما من اینک عهد من با توست و توپدر امت های بسیار خواهی بود.۴
5 Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
و نام تو بعد ازاین ابرام خوانده نشود بلکه نام تو ابراهیم خواهدبود، زیرا که تو را پدر امت های بسیار گردانیدم.۵
6 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
و تو را بسیار بارور نمایم و امت‌ها از تو پدیدآورم و پادشاهان از تو به وجود آیند.۶
7 Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
و عهدخویش را در میان خود و تو، و ذریتت بعد از تو، استوار گردانم که نسلا بعد نسل عهد جاودانی باشد، تا تو را و بعد از تو ذریت تو را خدا باشم.۷
8 Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
وزمین غربت تو، یعنی تمام زمین کنعان را، به تو و بعد از تو به ذریت تو به ملکیت ابدی دهم، وخدای ایشان خواهم بود.»۸
9 Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
پس خدا به ابراهیم گفت: «و اما تو عهد مرا نگاه دار، تو و بعد از توذریت تو در نسلهای ایشان.۹
10 Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
این است عهد من که نگاه خواهید داشت، در میان من و شما و ذریت تو بعد از تو هر ذکوری از شما مختون شود،۱۰
11 Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
وگوشت قلفه خود را مختون سازید، تا نشان آن عهدی باشد که در میان من و شماست.۱۱
12 Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
هر پسرهشت روزه از شما مختون شود. هر ذکوری درنسلهای شما، خواه خانه زاد خواه زرخرید، ازاولاد هر اجنبی که از ذریت تو نباشد،۱۲
13 Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
هرخانه زاد تو و هر زر خرید تو البته مختون شود تاعهد من در گوشت شما عهد جاودانی باشد.۱۳
14 Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
واما هر ذکور نامختون که گوشت قلفه او ختنه نشود، آن کس از قوم خود منقطع شود، زیرا که عهد مرا شکسته است.»۱۴
15 Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
و خدا به ابراهیم گفت: «اما زوجه توسارای، نام او را سارای مخوان، بلکه نام او ساره باشد.۱۵
16 Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
و او را برکت خواهم داد و پسری نیز ازوی به تو خواهم بخشید. او را برکت خواهم داد وامتها از وی به وجود خواهند آمد، و ملوک امتهااز وی پدید خواهند شد.»۱۶
17 Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
آنگاه ابراهیم به روی در‌افتاده، بخندید و در دل خود گفت: «آیابرای مرد صد ساله پسری متولد شود و ساره درنود سالگی بزاید؟»۱۷
18 Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
و ابراهیم به خدا گفت: «کاش که اسماعیل در حضور تو زیست کند.»۱۸
19 Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
خدا گفت: «به تحقیق زوجه ات ساره برای توپسری خواهد زایید، و او را اسحاق نام بنه، و عهدخود را با وی استوار خواهم داشت، تا با ذریت اوبعد از او عهد ابدی باشد.۱۹
20 Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
و اما در خصوص اسماعیل، تو را اجابت فرمودم. اینک او را برکت داده، بارور گردانم، و او را بسیار کثیر گردانم. دوازده رئیس از وی پدید آیند، و امتی عظیم ازوی بوجود آورم.۲۰
21 Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
لکن عهد خود را با اسحاق استوار خواهم ساخت، که ساره او را بدین وقت در سال آینده برای تو خواهد زایید.»۲۱
22 Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
و چون خدا از سخن‌گفتن با وی فارغ شد، از نزد ابراهیم صعود فرمود.۲۲
23 Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
و ابراهیم پسر خود، اسماعیل وهمه خانه زادان و زرخریدان خود را، یعنی هرذکوری که در خانه ابراهیم بود، گرفته، گوشت قلفه ایشان را در همان روز ختنه کرد، چنانکه خدا به وی امر فرموده بود.۲۳
24 Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
و ابراهیم نود و نه ساله بود، وقتی که گوشت قلفه‌اش مختون شد.۲۴
25 ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
و پسرش، اسماعیل سیزده ساله بود هنگامی که گوشت قلفه‌اش مختون شد.۲۵
26 Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
در همان روزابراهیم و پسرش، اسماعیل مختون گشتند.۲۶
27 Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.
وهمه مردان خانه‌اش، خواه خانه زاد، خواه زرخرید از اولاد اجنبی، با وی مختون شدند.۲۷

< Genesis 17 >