< Ezara 7 >
1 Zitatha izi, Aritasasita ali mfumu ya ku Perisiya, panali wansembe wina dzina lake Ezara. Iyeyu abambo ake anali Seraya mwana wa Azariya, mwana wa Hilikiya,
А по цих приго́дах, за царюва́ння Артаксеркса, царя перського, Е́здра, син Азарії, сина Хійлкійї,
2 mwana wa Salumu, mwana wa Zadoki, mwana wa Ahitubi,
сина Шаллуна, сина Садока, сина Ахітуви,
3 mwana wa Amariya, mwana wa Azariya, mwana wa Merayoti,
сина Амарії, сина Азарії, сина Мерайота,
4 mwana wa Zerahiya, mwana wa Uzi, mwana wa Buki,
сина Захарія, сина Уззі, сина Буккі,
5 mwana wa Abisuwa, mwana wa Finehasi, mwana wa Eliezara, mwana wa Aaroni mkulu wa ansembe uja.
сина Авішуї, сина Пінхаса, сина Елеазара, сина Аарона, первосвященика, —
6 Ezara ameneyu anabwera kuchokera ku Babuloni. Iyeyu anali wophunzira kwambiri za malamulo a Mose, amene Yehova Mulungu wa Israeli anapereka. Mfumu inamupatsa chilichonse chimene anapempha pakuti dzanja la Yehova Mulungu wake linali pa iye.
цей Ездра вийшов із Вавилону, а він був учитель, знаве́ць Мойсеєвого Зако́ну, що його дав Господь, Бог Ізраїлів. І дав йому цар згідно з тим, як була́ на ньому рука Господа, Бога його, всяке його пожада́ння.
7 Tsono mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wa Aritasasita, Ezara pamodzi ndi Aisraeli ena, kuphatikizapo ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda, ndi anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ananyamuka kubwerera ku Yerusalemu.
І пішли з ним дехто з Ізраїлевих синів, і з священиків, і Левитів, і співаків, і придве́рних, і храмови́х підда́нців до Єрусалиму сьомого року царя Артаксе́ркса.
8 Ezara anafika ku Yerusalemu pa mwezi wachisanu wa chaka chachisanu ndi chiwiri cha mfumu.
І прибув він до Єрусалиму п'ятого місяця, а то сьомий рік царюва́ння.
9 Iye anayamba ulendo wochoka ku Babuloni pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, ndipo anafika ku Yerusalemu pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu chifukwa dzanja labwino la Mulungu wake linali pa iye.
Бо першого дня місяця першого був поча́ток ви́ходу з Вавилону, а першого дня п'ятого місяця він прийшов до Єрусалиму, бо рука його Бога була добра на ньому.
10 Popeza Ezara anadzipereka kuwerenga ndi kusunga malamulo a Yehova, iye anafunitsitsa kuphunzitsa Aisraeli malamulo ndi malangizo a Mulungu.
Бо Ездра пригото́вив своє серце дослі́джувати Господнього Зако́на, і виконувати його, і навчати в Ізраїлі устава та права.
11 Iyi ndi kalata imene mfumu Aritasasita anapereka kwa wansembe Ezara, mlembi wa malamulo, munthu wophunzira kwambiri zokhudza malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
А оце ві́дпис писа́ння, що цар Артаксе́ркс дав священикові Ездрі, учителеві, що пише слова́ заповідей Господа та Його устави над Ізраїлем:
12 Ndine Aritasasita, mfumu ya mafumu. Ndikulembera iwe Ezara wansembe ndi mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba. Malonje.
„Артаксе́ркс, цар над царями, до священика Ездри, доскона́лого вчителя Зако́ну Бога Небесного, і так далі.
13 Tsopano ndikulamula kuti Mwisraeli aliyense, wansembe kapena Mlevi wokhala mʼdziko langa, amene akufuna kupita ku Yerusalemu ndi iwe, apite.
А ось ви́даний від мене нака́з, щоб кожен, хто в моїм царстві з Ізраїлевого наро́ду, і їхніх священиків, і Левитів з доброї волі бажає йти до Єрусалиму з тобою, нехай іде,
14 Ine mfumu pamodzi ndi alangizi anga asanu ndi awiri tikukutumani kuti mukafufuze za dziko la Yuda ndi mzinda wa Yerusalemu kuti mukaone mmene anthu akutsatira malamulo a Mulungu wanu, amene anawapereka kwa inu.
через те, що ти по́сланий від царя та семи його дора́дників, щоб дослідити про Юдею та про Єрусалим за правом твого Бога, правом, що в руці твоїй,
15 Utenge siliva ndi golide zimene ine mfumu ndi alangizi anga tapereka mwa ufulu kwa Mulungu wa Israeli, amene amakhala ku Yerusalemu.
і щоб відпра́вити срібло та золото, що цар та дорадники його поже́ртвували для Бога Ізраїлевого, Якого місце перебування в Єрусалимі,
16 Mutengenso siliva yense ndi golide amene mungamupeze mʼdziko lonse la Babuloni, ngakhalenso zinthu zimene anthu pamodzi ndi ansembe adzapereka mwaufulu kuperekera ku Nyumba ya Mulungu wawo ya ku Yerusalemu.
і все срібло та золото, яке ти зна́йдеш у всій вавилонській окру́зі ра́зом із пожертвами народу та священиків, які же́ртвують для дому їхнього Бога, що в Єрусалимі.
17 Ndi ndalama zimenezi mudzaonetsetse kuti mwagula ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa aamuna pamodzi ndi zopereka zake za chakudya ndi za chakumwa. Mudzapereke zimenezi pa guwa lansembe la Nyumba ya Mulungu wanu ya ku Yerusalemu.
Тому́ ти невідкладно купиш за це срібло биків, баранів, овечок, і їх жертви хлі́бні та їх жертви ливні, і принесе́ш їх на же́ртівнику дому вашого Бога, що в Єрусалимі.
18 Ndalama zotsala mudzagwiritse ntchito zimene inuyo ndi abale anu zikakukomerani malingana nʼkufuna kwa Mulungu wanu.
А що тобі та браттям твоїм буде добре вчинити з рештою срібла та золота, те зробі́ть за вподо́банням вашого Бога.
19 Ziwiya zonse zimene akupatsani kuti mukatumikire nazo mʼNyumba ya Mulungu wanu, kaziperekeni kwa Mulungu ku Yerusalemu.
А по́суд, що даний тобі на слу́ження дому твого Бога, віддай у цілості перед Богом Єрусалиму.
20 Ndipo chilichonse chimene chingafunike mʼNyumba ya Mulungu wanu, chimene mudzapeze mpata wopereka, ndalama zake zogulira zidzachokere mʼthumba la chuma cha mfumu.
А решта потрібного для дому Бога твого, що випаде тобі дати, буде да́на з дому царськи́х скарбів.
21 Tsopano Ine, mfumu Aritasasita, ndikulamula asungichuma onse a dera la Patsidya pa Yufurate kuti, chilichonse chimene wansembe Ezara, mlembi wa malamulo a Mulungu Wakumwamba adzapempha kwa inu, mupatseni mwa msanga.
А від мене — я цар Артаксеркс — ви́даний нака́з для всіх скарбникі́в, що в Заріччі, що все, чого зажадає від вас священик Ездра, учитель Зако́ну Бога Небесного, нехай буде докладно зро́блене:
22 Ngakhale atafunika makilogalamu 3,400 asiliva, makilogalamu 10,000 a tirigu, malita 2,000 a vinyo, malita 2,000 a mafuta ndi mchere wochuluka motani, zonsezi mupereke monga zingafunikire.
срібла — аж до сотні тала́нтів, і пшениці аж до сотні ко́рів, і вина аж до сотні ба́тів, і оливи аж до сотні батів, а соли — без за́пису.
23 Chimene Mulungu Wakumwamba walamula, chichitike mosamalitsa ku Nyumba ya Mulungu Wakumwamba kuopa kuti mkwiyo wa Mulungu ungayakire mfumu, dziko lake ndi ana ake.
Усе, що з нака́зу Небесного Бога, нехай буде горливо зро́блене для дому Небесного Бога, бо на́що був би гнів на царство царя та на синів його?
24 Tikukudziwitsaninso kuti kudzakhala kosaloledwa kukhometsa msonkho uliwonse anthu awa: ansembe, Alevi, oyimba nyimbo, alonda kapena aliyense wogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu.
І вас завідомля́ємо, що всі священики та Левити, співаки́, придве́рні, храмові́ підда́нці та працівники того Божого дому вільні, — дани́ни, пода́тку, чи ми́та не належить накладати на них!
25 Ndipo iwe, Ezara, monga mwa nzeru za Mulungu wako zimene uli nazo, usankhe oyendetsa zinthu ndi oweruza kuti azilamulira anthu onse okhala ku dera la Patsidya pa Yufurate, onse amene amadziwa malamulo a Mulungu wako. Ndipo uphunzitse aliyense amene sawadziwa.
А ти, Ездро, за мудрістю Бога твого, яка в руці твоїй, попризнача́й су́ддів та викона́вців Зако́ну, щоб судили для всього народу, що в Заріччі, для всіх, хто знає зако́ни твого Бога, а хто не знає, тих навчите́.
26 Ndipo amene sadzamvera lamulo la Mulungu wako ndi lamulo la mfumu alangidwe kolimba kapena aphedwe kapena achotsedwe mʼdzikolo, kapena katundu wake alandidwe, kapena aponyedwe mʼndende.
А кожен, хто не буде виконувати Зако́на твого Бога та зако́на царсько́го докладно, щоб чинився над ним суд: чи то на смерть, чи то на вигна́ння, чи то на кару маєткову, чи то на ув'я́знення“.
27 Ezara anati atamandike Yehova, Mulungu wa makolo athu, amene wayika ichi mu mtima wa mfumu kuti alemekeze Nyumba ya Yehova ya ku Yerusalemu mʼnjira imeneyi.
Благословенний Господь, Бог наших батьків, що вклав у царе́ве серце, щоб оздо́бити дім Господній, що в Єрусалимі,
28 Ameneyonso waonetsa chikondi chake chosasinthika kwa ine pamaso pa mfumu, alangizi ake ndi nduna zake zamphamvu kuti andikomere mtima. Choncho ndinalimba mtima popeza Yehova, Mulungu wanga anali nane, ndipo ndinasonkhanitsa atsogoleri ambiri a Israeli kuti apite nane pamodzi.
а на мене нахили́в милість перед царем та його дора́дниками, та всіма́ хоробрими царе́вими зве́рхниками! А я зміцни́вся, бо рука Господа, Бога, була надо мною, і я зібрав провідни́х людей з Ізраїля, щоб вони пішли зо мною.