< Eksodo 23 >
1 “Usafalitse mbiri yabodza. Usathandize munthu wolakwa pomuchitira umboni wonama.
Не будеш розносити неправдивих поголосок. Не покладеш руки своєї з несправедливим, щоб бути свідком неправди.
2 “Usatsate gulu la anthu ndi kuchita choyipa. Pamene ukupereka umboni mʼbwalo lamilandu, usakhotetse mlandu chifukwa chofuna kukondweretsa anthu ambiri.
Не будеш з більшістю, щоб чинити зло. І не будеш висловлюватися про по́зов, прихиляючись до більшости, щоб перегнути правду.
3 Ndipo poweruza mlandu wa munthu wosauka usamukondere.
І не будеш потура́ти вбогому в його по́зові.
4 “Ngati ukumana ndi ngʼombe kapena bulu wa mdani wako zitasochera, uwonetsetse kuti wazitenga kupita nazo kwa mwini wakeyo.
Коли стрінеш вола свого ворога або осла його, що заблудив, то конче повернеш його йому.
5 Ngati uwona bulu wa munthu wina amene amakuda atagwa ndi katundu, usamusiye pomwepo, uwonetsetse kuti wamuthandiza.
Коли побачиш осла свого ворога, що лежить під тягаре́м своїм, то не зага́їшся помогти йому, — конче поможеш ра́зом із ним.
6 “Usakhotetse milandu ya anthu osauka.
Не перегинай суду на бік вбогого свого́ в його по́зові.
7 Upewe zabodza ndipo usaphetse munthu wosalakwa ndi wolungama, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
Від неправдивої справи відда́лишся, а чистого й справедливого не забий, бо Я не всправедливлю несправедливого.
8 “Musamalandire chiphuphu, pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu oweruza ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
А хабара́ не візьмеш, бо хаба́р осліплює зрячих і викривляє слова справедливих.
9 “Usamuzunze mlendo, pakuti inu nomwe mukudziwa mmene amamvera mlendo chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Igupto.
А прихо́дька не будеш тиснути, бож ви познали душу прихо́дька, бо самі були прихо́дьками в єгипетськім кра́ї.
10 “Muzidzala mbewu zanu mʼmunda ndi kumakolola mbewuzo kwa zaka zisanu ndi chimodzi.
І шість літ будеш сі́яти землю свою, і будеш збирати її врожай,
11 Koma chaka chachisanu ndi chiwiri muzisiya osalima mindayo kuti anthu osauka pakati panu azipezamo chakudya, ndipo nyama zakuthengo zizidya zotsalazo. Muzichita chimodzimodzi ndi minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi.
а сьомого — опустиш її та полишиш її, і будуть їсти вбогі народу твого, а позостале по них буде їсти польова́ звірина́. Так само зробиш для виноградинка твого, і для оливки твоєї.
12 “Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.
Шість день будеш робити діла́ свої, а сьомого дня спочи́неш, щоб відпочив віл твій, і осел твій, і щоб відідхнув син невільниці твоєї й прихо́дько.
13 “Samalani pochita zonse zimene ine ndanena. Musamapemphere kwa milungu ina ndipo mayina awo musamawatchule.
І все, що Я сказав вам, будете вико́нувати. А йме́ння інших богів не згадаєте, — не буде почуте воно на устах твоїх.
14 “Muzichita zikondwerero zolemekeza Ine katatu pa chaka.
Три ра́зи на рік будеш святкува́ти Мені.
15 “Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.
Будеш дотримувати свято Опрі́сноків; сім день будеш їсти опрісноки, як наказав тобі, окресленого часу місяця авіва, бо в нім ти був вийшов з Єгипту. І не будете являтися перед лицем Моїм з порожніми руками.
16 “Muzichita Chikondwerero cha Masika pogwiritsa ntchito zipatso zoyambirira kucha zimene munadzala mʼmunda. “Muzichitanso Chikondwerero cha Zokolola pakutha pa chaka, pamene mukututa zokolola zanu mʼmunda.
І свято жнив первопло́ду праці твоєї, що сієш на полі. І свято збира́ння при закінченні року, коли ти збираєш з поля працю свою.
17 “Amuna onse azionekera pamaso pa Ambuye Yehova katatu pa chaka.
Три рази на рік буде являтися ввесь чоловічий рід твій перед лицем Владики Господа.
18 “Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti. “Ndipo musasunge mafuta anyama yansembe ya pa chikondwerero mpaka mmawa.
Не будеш прино́сити крови жертви Моєї на квашенім, а лій Моєї святкової жертви не буде ночува́ти аж до ра́нку.
19 “Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku Nyumba ya Yehova Mulungu wanu. “Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Поча́тки первопло́ду твоєї землі принесеш до дому Господа, Бога твого. Не будеш варити ягняти в молоці його матері.
20 “Taona Ine ndikutuma mngelo wanga patsogolo panu kuti akutetezeni mʼnjiramo ndi kukakufikitsani ku malo amene ndakonza.
Ось Я посилаю Ангола перед лицем твоїм, щоб він охороня́в у дорозі тебе, і щоб провадив тебе до того місця, яке Я пригото́вив.
21 Muzimumvera ndi kumvetsetsa zimene akunena. Musamuwukire chifukwa sadzakhululuka kuwukira kwanu, pakuti akuchita zimenezi mʼdzina langa.
Стережися перед лицем Його, і слухайся Його голосу! Не протився Йому, бо Він не проба́чить вашого гріха, — бо Ім'я́ Моє в Ньому
22 Ngati mudzamvera iyeyu ndi kuchita zonse zimene Ine ndikunena, Ine ndidzakhala mdani wa adani anu ndipo ndidzatsutsana ndi onse otsutsana nanu.
Коли ж справді послухаєш ти Його голосу, і вчиниш усе, що говорю́, то Я буду ворогува́ти проти ворогів твоїх, і буду гноби́ти твоїх гноби́телів.
23 Mngelo wanga adzakhala patsogolo panu ndipo adzakufikitsani mʼdziko la Aamori, Ahiti, Aperezi, Akanaani, Ahivi ndi Ayebusi, ndipo ndidzawapheratu onsewo.
Бо Мій Ангол ходитиме перед лицем твоїм, і запрова́дить тебе до амореянина, і хіттеянина, і періззеянина, і ханаанеянина, хіввеянина, і євусеянина, — а Я зни́щу його.
24 Musagwadire milungu yawo kapena kuyipembedza. Ndipo musatsatire zinthu zomwe amachita. Koma inu mukawononge milungu yawo ndi kuphwasula malo amene amapembedzerapo.
Не будеш вклонятися їхнім бога́м, і служити їм не будеш, і не будеш чинити за вчинками їх, бо конче порозбиваєш і конче поламаєш їхні стовпи́ для богів.
25 Muzipembedza Yehova Mulungu wanu ndipo adzakudalitsani ndi chakudya ndi madzi ndiponso ndidzachotsa nthenda pakati panu.
І будеш служити ти Господе́ві, Богові своєму, і Він поблагосло́вить твій хліб та воду твою, і з-посеред тебе усуне хворо́бу.
26 Palibe mkazi amene adzapite padera kapena kukhala wosabereka mʼdziko mwanu. Ndidzakupatsani moyo wautali.
У твоїм кра́ї не буде такої, що скидає плода́, ані неплідної. Число твоїх днів Я доповню.
27 “Ine ndidzawachititsa mantha ndi kusokoneza anthu onse amene adzalimbana ndi inu ndipo adani anu onse adzakuthawani.
Свій страх пошлю перед лицем твоїм, і приведу в замішання ввесь цей наро́д, що ти ввійдеш між ньо́го. І всіх ворогів твоїх оберну́ до тебе поти́лицею.
28 Ahivi, Akanaani ndi Ahiti adzathawa ngati kuti ndawatumizira mavu.
І пошлю ше́ршня перед тобою, і він вижене перед тобою хіввеянина, ханаанеянина та хіттеянина.
29 Komabe sindidzawachotseratu onse mʼchaka chimodzi chifukwa dziko lingadzakhale lopanda anthu ndipo nyama zakuthengo zidzakuchulukirani.
Не вижену їх перед тобою в однім році, щоб не став той край спусто́шеним, і не розмно́жилася на тебе польова́ звірина́.
30 Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.
Помалу Я буду їх виганяти перед тобою, аж поки ти розро́дишся, і пося́деш цей край.
31 “Malire a dziko lanu adzakhala kuyambira ku Nyanja Yofiira mpaka ku nyanja ya Afilisti, ndiponso kuyambira ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yufurate. Anthu onse okhala mʼdziko limeneli ndidzawapereka mʼmanja mwanu ndipo mudzawathamangitsa.
І покладу́ границю твою від моря Червоного й аж до моря Филистимського, і від пустині аж до річки, бо дам в вашу руку ме́шканців цього кра́ю, — і ти виженеш їх перед собою.
32 Musachite pangano ndi iwo kapena ndi milungu yawo.
Не складай умови з ними та з їхніми бога́ми.
33 Asadzakhale mʼdziko lanu chifukwa angadzakuchimwitseni ndi kuyamba kupembedza milungu yawo. Mukadzatero ndiye kuti mwakodwa mu msampha.”
Не бу́дуть сидіти вони в твоїм кра́ї, щоб не ввести тебе в гріх супроти Мене, коли будеш служити їхнім бога́м, бо це буде па́стка тобі!“