< Estere 4 >

1 Mordekai atamva zonse zimene zinachitika, anangʼamba zovala zake, navala chiguduli ndi kudzola phulusa, ndipo analowa mu mzinda, akulira mokweza ndi mowawidwa mtima.
و چون مردخای از هرآنچه شده بود اطلاع یافت، مردخای جامه خود را دریده، پلاس با خاکستر در بر کرد و به میان شهر بیرون رفته، به آواز بلند فریاد تلخ برآورد.۱
2 Ndipo anapita ndi kuyima pa chipata cha mfumu, chifukwa panalibe wina aliyense amaloledwa kulowa pa chipata cha mfumu atavala chiguduli.
و تاروبروی دروازه پادشاه آمد، زیرا که جایز نبود که کسی با لباس پلاس داخل دروازه پادشاه بشود.۲
3 Chigawo chilichonse kumene mawu a mfumu ndi lamulo lake zinafika, kunali maliro akulu pakati pa Ayuda. Iwo ankasala zakudya, kulira mofuwula ndi kumadandaula. Ambiri anavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
و در هر ولایتی که امر و فرمان پادشاه به آن رسید، یهودیان را ماتم عظیمی و روزه و گریه ونوحه گری بود و بسیاری در پلاس و خاکسترخوابیدند.۳
4 Anamwali otumikira mfumukazi Estere ndi adindo ake ofulidwa atabwera ndi kumuwuza za Mordekai, anavutika kwambiri. Estere anamutumizira zovala kuti avale ndi kuti avule chiguduli chake koma Mordekai sanalole zimenezo.
پس کنیزان و خواجه‌سرایان استر آمده، اورا خبر دادند و ملکه بسیار محزون شد و لباس فرستاد تا مردخای را بپوشانند و پلاس او را ازوی بگیرند، اما او قبول نکرد.۴
5 Kenaka Estere anayitana Hataki, mmodzi wa adindo a mfumu ofulidwa amene anayikidwa kuti azimutumikira kuti apite kwa Mordekai kuti akamve chimene chimamuvuta komanso chifukwa chochitira zimenezi.
آنگاه استر، هتاک را که یکی از خواجه‌سرایان پادشاه بود و او را به جهت خدمت وی تعیین نموده بود، خواند و او راامر فرمود که از مردخای بپرسد که این چه امراست و سببش چیست.۵
6 Choncho Hataki anapita kwa Mordekai ku bwalo la mzinda patsogolo pa chipata cha mfumu.
پس هتاک به سعه شهرکه پیش دروازه پادشاه بود، نزد مردخای بیرون رفت.۶
7 Mordekai anamuwuza zonse zimene zinamuchitikira kuphatikizapo mtengo weniweni wa ndalama zimene Hamani analonjeza kupereka mosungira chuma cha mfumu za anthu amene adzawononge a Yuda.
و مردخای او را از هرچه به او واقع شده واز مبلغ نقره‌ای که هامان به جهت هلاک ساختن یهودیان وعده داده بود که آن را به خزانه پادشاه بدهد، خبر داد.۷
8 Mordekai anamupatsanso imodzi mwa makalata a ulamuliro wonena za chiwembuchi amene anawasindikiza ku Susa kukamuonetsa ndi kumufotokozera zonse Estere. Anamuwuzanso kuti akamudandaulire kuti akapite kwa mfumu kukapempha chifundo ndi kuyidandaulira chifukwa cha anthu a mtundu wake.
و سواد نوشته فرمان را که درشوشن به جهت هلاکت ایشان صادر شده بود، به او داد تا آن را به استر نشان دهد و وی را مخبرسازد و وصیت نماید که نزد پادشاه داخل شده، ازاو التماس نماید و به جهت قوم خویش از وی درخواست کند.۸
9 Hataki anabwerera ndi kumufotokozera Estere zimene Mordekai ananena.
پس هتاک داخل شده، سخنان مردخای را به استر بازگفت.۹
10 Ndipo Estere anamutuma Hataki kuti akanene kwa Mordekai kuti,
و استر هتاک را جواب داده، او راامر فرمود که به مردخای بگوید۱۰
11 “Atumiki onse amfumu ndi anthu a zigawo za mfumu ankadziwa kuti mwamuna kapena mkazi aliyense akalowa ku bwalo lake la mʼkati mosayitanidwa ndi mfumu pali lamulo limodzi: lamuloli ndi lakuti aphedwe. Zimasintha pokhapokha ngati mfumu iloza munthuyo ndi ndodo yagolide kuti akhale ndi moyo. Koma papita masiku makumi atatu ndisanayitanidwe ndi mfumu.”
که «جمیع خادمان پادشاه و ساکنان ولایتهای پادشاه می‌دانند که به جهت هرکس، خواه مرد و خواه زن که نزد پادشاه به صحن اندرونی بی‌اذن داخل شود، فقط یک حکم است که کشته شود، مگرآنکه پادشاه چوگان زرین را بسوی او دراز کند تازنده بماند. و سی روز است که من خوانده نشده‌ام که به حضور پادشاه داخل شوم.»۱۱
12 Tsono Mordekai anawuzidwa mawu a Estere.
پس سخنان استر را به مردخای باز‌گفتند.۱۲
13 Kenaka Mordekai anawawuza kuti akamuyankhe Estere motere: “Usaganize kuti iwe wekha mwa Ayuda onse udzapulumuka chifukwa chakuti uli mʼnyumba ya mfumu.
و مردخای گفت به استر جواب دهید: «در دل خود فکر مکن که تو در خانه پادشاه به خلاف سایر یهود، رهایی خواهی یافت.۱۳
14 Pakuti ngati ukhalatu chete nthawi ino, chithandizo ndi chipulumutso cha Ayuda zidzachokera kwina nʼkutheka kuti iwe ndi a pa banja la makolo ako mudzafa. Ndipo adziwa ndani mwina unalowa ufumu chifukwa cha nthawi ngati imeneyi?”
بلکه اگر در این وقت تو ساکت بمانی، راحت و نجات برای یهود از جای دیگر پدید خواهد شد. اما تو وخاندان پدرت هلاک خواهید گشت و کیست بداند که به جهت چنین وقت به سلطنت نرسیده‌ای.»۱۴
15 Pamenepo Estere anatumiza yankho ili kwa Mordekai:
پس استر فرمود به مردخای جواب دهید۱۵
16 “Pitani, mukasonkhanitse pamodzi Ayuda onse amene ali mu Susa ndipo mundisalire chakudya. Musadye kapena kumwa kwa masiku atatu, usiku ndi usana. Ine ndi anamwali anga onditumikira tidzasala chakudya monga inu. Izi zikachitika, ine ndidzapita kwa mfumu, ngakhale kutero ndikutsutsana ndi lamulo. Ndipo ngati nʼkufa ndife ndithu.”
که «برو و تمامی یهود را که در شوشن یافت می‌شوند جمع کن و برای من روزه گرفته، سه شبانه‌روز چیزی مخورید و میاشامید و من نیز باکنیزانم همچنین روزه خواهیم داشت. و به همین طور، نزد پادشاه داخل خواهم شد، اگر‌چه خلاف حکم است. و اگر هلاک شدم، هلاک شدم.»۱۶
17 Choncho Mordekai anapita ndi kuchita monga Estere anamupemphera.
پس مردخای رفته، موافق هرچه استر وی را وصیت کرده بود، عمل نمود.۱۷

< Estere 4 >