< 2 Mafumu 20 >

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
Тими днями смертельно захворі́в був Єзекія. І прийшов до нього Іса́я, Амо́сів син, пророк, і сказав до нього: „Так сказав Господь: Заряди своїм домом, бо ти вмреш, а не ви́дужаєш“.
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
А той відвернув обличчя своє до стіни, і помолився до Господа, говорячи:
3 “Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
„О, Господи, згадай же, що я ходив перед лицем Твоїм правдою та ці́лим серцем, і робив я добре в оча́х Твоїх“. І заплакав Єзекія ревним плаче́м.
4 Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
І сталося, Ісая не вийшов ще з сере́дини міста, а до нього було Господнє слово, говорячи:
5 “Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
„Вернися, і скажеш до Єзекії, володаря Мого народу: Так сказав Господь, Бог батька твого Давида: Почув Я молитву твою, побачив Я сльозу́ твою! Ось Я вилікую тебе, — третього дня зі́йдеш ти до Господнього дому!
6 Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
І до днів твоїх Я дода́м п'ятнадцять літ, і з руки асирійського царя врятую тебе та це місто, й обороню́ це місто ради Себе та ради раба Свого Давида“.
7 Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
А Ісая сказав: „Візьміть грудку фіґ“. І взяли́ й поклали на того гнояка́, — і він ви́дужав...
8 Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
І сказав Єзекія до Ісаї: „Який знак, що Господь мене ви́лікує, і що я третього дня зійду́ до Господнього дому?“
9 Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
І сказав Ісая: „Ось тобі знак той від Господа, що Господь зробить ту річ, про яку говорив: Чого хочеш, — щоб пішла тінь уперед на десять ступені́в, чи щоб верну́лася на десять ступені́в?“
10 Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
І сказав Єзекія: „Легко тіні похили́тися вперед на десять ступені́в; ні, — а нехай тінь ве́рнеться назад на десять ступені́в!“
11 Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
І кли́кнув пророк Ісая до Господа, і Він заверну́в тінь на ступеня́х, де вона спускалася на ступені́ Ахазові, на десять ступені́в...
12 Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
Того ча́су послав Беродах-Бал'адан, син Бал'аданів, вавилонський цар, листа́ та дару́нка до Єзекії, бо прочув був, що Єзекія захворі́в.
13 Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
І вислухав їх Єзекія, і показав їм усю скарбни́цю свою, — і срібло, і золото, і па́хощі, і добру оливу, і всю зброївню свою, і все, що знахо́дилося в його скарбницях. Не було речі, якої не показав би їм Єзекія в домі своїм та в усім володі́нні своїм.
14 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
І прийшов пророк Іса́я до царя Єзекії та й сказав до нього: „Що́ говорили ці люди? І звідки вони прийшли до тебе?“А Єзекія сказав: „Вони прийшли з далекого кра́ю, з Вавилону“.
15 Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
І той сказав: „Що́ вони бачили в домі твоїм?“І Єзекія сказав: „Усе, що в домі моїм, вони бачили, — не було речі, якої не показав би я їм у скарбни́цях своїх“,
16 Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
I сказав Ісая до Єзекії: „Послухай Господнього слова:
17 Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
Ось прихо́дять дні, і все, що́ в домі твоєму, і що були зібрали батьки твої аж до цього дня, буде ви́несене до Вавилону. Нічого не позоста́неться, говорить Господь!
18 Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
А з синів твоїх, що вийдуть із тебе, яких ти поро́диш, де́кого заберуть, — і вони будуть є́внухами в палатах вавилонського царя!“
19 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
І сказав Єзекія до Ісаї: „Добре Господнє слово, яке ти сказав!“І подумав собі: „Так, мир та безпека буде за моїх днів!“
20 Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
А решта діл Єзекії та вся лица́рськість його, і як він зробив ста́ва та водотя́га, і впровадив воду до міста, — ото вони написані в Книзі Хроніки Юдиних царів.
21 Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
І спочив Єзекія зо своїми батьками, а замість нього зацарював син його Манасі́я.

< 2 Mafumu 20 >