< 2 Mbiri 29 >
1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
Єзекі́я зацарював у віці двадцяти́ й п'яти́ літ, а двадцять і дев'ять літ царював він в Єрусалимі. А ім'я́ його матері — Авійя, дочка́ Захарії.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
І робив він угодне в Господніх оча́х, як усе, що робив був його ба́тько Давид.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
Він першого року свого царюва́ння, місяця першого відчини́в двері Господнього дому, і попра́вив їх.
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
І привів він священиків та Левитів, і зібрав їх на схі́дню пло́щу,
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
та й сказав їм: „Послухайте мене, Левити! Освяті́ться тепер, і освятіть дім Господа, Бога ваших батьків, і ви́несіть нечисть із святині.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
Бо наші батьки сироневі́рилися, і робили лихе́ в оча́х Господа, Бога нашого, і залишили Його, і відвернули своє обличчя від Господньої скинії, й обернулися спи́ною до неї.
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
Також замкну́ли вони двері притво́ру, і погасили лямпа́дки, а кадила не кадили, і цілопа́лення не прино́сили в святині для Ізраїлевого Бога.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
І був Господній гнів на Юду та на Єрусалим, і Він дав їх на га́ньбу, і на спусто́шення, і на посміхо́вище, як ви бачите своїми очи́ма.
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
І ось попа́дали наші батьки від меча, а наші сини, і наші до́чки, і жінки наші в неволі за це!
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Тепер на моєму серці лежить скла́сти заповіта з Господом, Ізра́їлевим Богом, — і нехай Він відве́рне від нас жар гніву Свого.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
Сини мої, не будьте недбалі тепер, бо вас Господь вибрав ставати перед лицем Його на службу Йому, та щоб служити Йому й кадити Йому!“
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
І встали Левити: Махат, син Амасаїв, і Йоїл, син Азарії, від синів Кегатових; а від синів Мерарієвих: Кіш, син Авдіїв, і Азарія, син Єгаллел'їлів; а від Ґершонівців: Йоах, син Зіммин, і Еден, син Йоахів;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
а від синів Еліцафанових: Шімрі, і Єіїл; а від синів Асафових: Захарій та Маттанія.
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
А від Геманових синів: Єхіїл, і Шім'ї; а від синів Єдутунових: Шемая та Уззіїл.
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
І зібрали вони братів своїх, і освятилися, і пішли за нака́зом царськи́м у справах Господніх, щоб очистити Господній дім.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
І повхо́дили священики до сере́дини Господнього дому на очи́щення. І повино́сили вони всю нечистість, яку знайшли в Господньому храмі, до подвір'я Господнього дому, а Левити взяли́ це, щоб винести назо́вні до долини Кедро́н.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
І зачали́ вони першого дня першого місяця освящати, а восьмого дня того місяця ввійшли до Господнього притво́ру. І освятили вони Господній дім за вісім день, а шістнадцятого дня першого місяця закінчи́ли.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
І ввійшли вони в сере́дину дому до царя Єзекії та й сказали: „Очистили ми ввесь Господній дім, і же́ртівника цілопа́лення, та всі його речі, і стіл укладання хлібі́в та всі його речі.
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
А всі ті речі, які цар Ахаз занеха́в був за свого царюва́ння, коли спроневі́рився, ми приготовили та освятили, і ось вони перед Господнім же́ртівником“.
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
І встав рано цар Єзекія, і зібрав зверхників міста та й увійшов до Господнього дому.
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
І привели́ вони сім биків, і сім барані́в, і сім ове́чок, і сім козлів на жертву за гріх: за царство, і за святиню, і за Юду, а він звелів Ааро́новим синам, священикам, прине́сти це в жертву на Господньому же́ртівнику.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
І порізали ту велику худобу, а священики прийняли́ кров і покропи́ли на жертівника; і порізали баранів, і покропили ту кров на жертівника; і порізали ове́чок, і покропили ту кров на жертівника.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
І привели́ козлів жертви за гріх перед царя та збори, і вони поклали свої руки на них.
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
І зарізали їх священики, а їхньою кров'ю очи́стили жертівника, щоб очистити всього Ізраїля, бо за всього Ізраїля звелів цар принести це цілопа́лення та цю жертву за гріх.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
І поставив він Левитів Господнього дому з цимба́лами, з а́рфами та з ци́трами, за нака́зом Давида та Ґада, царе́вого прозорли́вця, та пророка Ната́на, бо в руці Господа наказ, що йде через пророків Його.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
І постава́ли Левити з Давидовим знаря́ддям, а священики — із су́рмами.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
І сказав Єзекі́я принести цілопа́лення на жертівника. А коли розпочали́ цілопа́лення, зачався спів Господе́ві та звуки су́рем і музи́чного знаря́ддя Давида, Ізраїлевого царя.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
І ввесь збір вклонився, і співаки́ співали, а су́рми сурми́ли, — це все аж до кінця цілопа́лення!
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
А як скінчи́ли прино́сити жертву, попа́дали навко́лішки цар та всі, що були з ним, і вклони́лися.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
І сказав цар Єзекія та зверхники до Левитів, щоб вони хвалили Господа словами Давида та прозорли́вця Асафа, — і вони хвалили з великою радістю, і схилялися, і вклоня́лися до землі.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
І відпові́в Єзекі́я й сказав: „Тепер ви освя́чені для Господа. Підійдіть, і приведі́ть жертви та при́носи вдячні для Господнього дому“. І привів збір жертви та при́носи вдячні, і кожен, хто мав жертве́нне серце, — прино́сив цілопа́лення.
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
І було число цілопа́лення, що спрова́див збір: худоби великої — сімдеся́т, барані́в — сотня, ове́чок — двісті, для цілопа́лення Господе́ві все це.
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
А для святости: худоби великої — шість сотень, а худоби дрібно́ї — три тисячі.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
Тільки священиків було мало, і не могли́ вони обдира́ти шкур зо всіх цілопа́лень; і допомага́ли їм їхні брати Левити аж до скі́нчення праці, і поки освятилися священики, бо Левити були простосердіші на освя́чення, аніж священики.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
І також було багато па́лень серед мирних жертов і серед жертов литих до цілопа́лення. І так була відновлена служба Господнього дому.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
І радів Єзекі́я та ввесь народ тим, що́ Бог приготовив для народу, бо та річ сталася несподі́вано!