< 1 Samueli 5 >

1 Afilisti atalanda Bokosi la Mulungu lija, analitenga kuchoka ku Ebenezeri kupita ku Asidodi.
Then the Philistims tooke the Arke of God and caried it from Eben-ezer vnto Ashdod,
2 Kenaka anatenga Bokosi la Chipanganolo nabwera nalo ku nyumba ya Dagoni ndi kuliyika pambali pa Dagoni.
Euen the Philistims tooke ye Arke of God, and brought it into the house of Dagon, and set it by Dagon.
3 Anthu a ku Asidodi atadzuka mmawa mwake, anangoona Dagoni atagwa pansi chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova! Iwo anatenga Dagoni ndi kumuyimika pamalo pake.
And when they of Ashdod rose the next day in the morning, beholde, Dagon was fallen vpon his face on the ground before the Arke of the Lord, and they tooke vp Dagon, and set him in his place againe.
4 Koma mmawa mwakenso atadzuka, anaona Dagoni atagwa chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova. Mutu wake ndi manja ake zinali zitaduka ndi kugwera pa khonde polowera, thunthu lake lokha ndilo linatsala.
Also they rose vp earely in the morning the next day, and beholde, Dagon was fallen vpon his face on the ground before the Arke of the Lord, and the head of Dagon and the two palmes of his hands were cut off vpon the thresholde: onely the stumpe of Dagon was left to him.
5 Nʼchifukwa chake mpaka lero ansembe a Dagoni kapena wina aliyense amene amalowa mʼkachisi wa Dagoni ku Asidodi saponda pa khonde.
Therefore the Priests of Dagon, and all that come into Dagons house tread not on the thresholde of Dagon in Ashdod, vnto this day.
6 Yehova analanga koopsa anthu a ku Asidodi. Yehova anawawononga ndi kuwazunza ndi zithupsa Asidoniwa pamodzi ndi anthu a madera ozungulira.
But the hand of the Lord was heauie vpon them of Ashdod, and destroyed them, and smote them with the emerods, both Ashdod, and the coastes thereof.
7 Anthu a ku Asidodi ataona zimene zimachitika anati, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lisakhale kuno chifukwa akutizunza ife pamodzi ndi mulungu wathu Dagoni.”
And when the men of Ashdod sawe this, they sayd, Let not the Arke of the God of Israel abide with vs: for his hand is sore vpon vs and vpon Dagon our god.
8 Choncho anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anawafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu wa Israeli tichite nalo chiyani?” Iwo anayankha kuti, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lipite ku Gati.” Kotero analichotsa Bokosi la Mulungu wa Israelilo.
They sent therefore and gathered all the princes of the Philistims vnto them, and sayde, What shall we doe with the Arke of the God of Israel? And they answered, Let the Arke of the God of Israel be caried about vnto Gath: and they caried the Arke of the God of Israel about.
9 Koma atafika nalo ku Gati, Yehova analanga mzindawo, ndipo anthu anachita mantha aakulu. Iye anazunza anthu a mu mzindawo, ana ndi akulu omwe, ndi zithupsa.
And when they had caried it about, the hand of the Lord was against the citie with a very great destruction, and he smote the men of the citie both small and great, and they had emerods in their secret partes.
10 Choncho anatumiza Bokosi la Mulungu ku Ekroni. Koma Bokosi la Mulungu lija litangofika ku Ekroni, anthu a ku Ekroni analira kuti, “Abwera nalo Bokosi la Mulungu wa Israeli kwa ife kuti atiphe pamodzi ndi anthu athu.”
Therefore they sent the Arke of God to Ekron: and assoone as the Arke of God came to Ekron, the Ekronites cryed out, saying, They haue brought the Arke of the God of Israel to vs to slay vs and our people.
11 Kotero iwo anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anati, “Chotsani Bokosi la Mulungu wa Israeli, libwerere ku malo ake. Tikapanda kutero lidzatipha ife ndi anthu athu.” Pakuti mu mzinda monse munali mantha aakulu kwambiri ndipo Mulungu ankawalanga kwambiri anthu a kumeneko.
Therefore they sent, and gathered together all the princes of the Philistims and sayd, Sende away the Arke of the God of Israel, and let it returne to his owne place, that it slay vs not and our people: for there was a destruction and death throughout all the citie, and the hand of God was very sore there.
12 Anthu amene sanafe anavutika ndi zithupsa, ndipo kulira kwa anthu a mu mzindamo kunamveka kumwamba.
And the men that dyed not, were smitten with the emerods: and the cry of the citie went vp to heauen.

< 1 Samueli 5 >