< 1 Petro 4 >
1 Popeza kuti Khristu anamva zowawa mʼthupi lake, mukhale nawonso mtima omwewo, chifukwa iye amene wamva zowawa mʼthupi lake walekana nawo uchimo.
Bara na Kristi na neo nan nya kidowo, nanere anung wang teren nibinai bara uniu uremme, vat nle na ana neo nan nya kidowo ana surto nan nya kulapi.
2 Chifukwa cha ichi, iwo sakhalanso moyo wawo akuchita zofuna za matupi awo, koma amachita chifuniro cha Mulungu.
Na unit une do nin lissosin nan nya ntok kidowo ba, ama na nya nsu Kutelle bara ngisin nayiri nlau me.
3 Pakuti mwataya kale nthawi yambiri mʼmbuyomu pochita zimene anthu osapembedza amachita, moyo wokhumba zonyansa, zilakolako zoyipa kuledzera, zochitika zoyipa za pa phwando, mapokoso ndi kupembedza mafano onyansa.
Bara kubi na kata Alumai gbardang nworu isu imon ile na ina di nin sun sue, upiziru nawani sa nanilime uhem, kuma niyizi, uso nadadu, avu ananzang, nin son toro, a udortun ncil.
4 Anthu osapembedza amadabwa pamene simuthamangira nawo kuchita zoyipitsitsazi, nʼchifukwa chake amakuchitani chipongwe.
Iwa kpiliza id imon ipesse na anung din su ile imone nan ghinu ba, inam wa su uliru unanzang nati mine
5 Koma adzafotokoza okha mlandu wawo kwa Mulungu amene wakonzeka kuweruza amoyo ndi akufa.
ko gha ma batuzu imon ile na asu kiti nle na ama su ushara nanan lai nin na nan kul.
6 Pa chifukwa chimenechi, Uthenga Wabwino unalalikidwa ngakhale kwa iwo amene tsopano ndi akufa, kuti adzaweruzidwe monga anthu ku thupi, koma adzakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mu mzimu.
Bara ile imonere iwa su uwaze kiti nale na ina kuzu, ina su ina malu isu nani ushara nan nya nidowo mine nafo anit, inan su lissosin nafo usu Nruhu Kutelle.
7 Chimaliziro cha zinthu zonse chili pafupi. Choncho khalani maso ndi odziletsa kuti muthe kupemphera.
Imalin nimone vat din cinu. Bara nani nonko ibinai mine, sun ukpiluzu mine nin nibinai nisheu bara nlira mine.
8 Koposa zonse muzikondana wina ndi mnzake kwambiri, chifukwa chikondi chimaphimba machimo ambiri.
A imon dutu vat, yitan nin su ugip kiti linuawana vat, bara na usu di nin su u yinin a lapi namong ba.
9 Muzisamalirana wina ndi mnzake osamanyinyirika.
Yitan nin su nsesu namara nan nya mine na nin kugbullu ba.
10 Aliyense agwiritse ntchito mokhulupirika mphatso iliyonse imene anayilandira potumikira ena ngati adindo ogwiritsa bwino ntchito mphatso za Mulungu za mitundumitundu.
Nafo na ko uyeme mine na seru ufillu, sun katwa mun nan nya nati mine, nafo a wakilai Kutelle acine na ina seru ufillu ngangang gbardang kiti Kutelle.
11 Ngati wina ayankhula, ayankhuledi mawu enieni a Mulungu. Ngati wina atumikira, atumikire ndi mphamvu imene Mulungu amapereka, kuti pa zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn )
Andi umong nsu uliru na uso nafo agbulang nliru Kutelle; andi umong din su katwa, na asu nafo nin likara na Kutelleri din nizu, bara nan nya nimon vat, na Kutelle se ngongong unuzu Yesu Kristi. Ngongong nin likara di unme vat sa ligan. Uso nani. (aiōn )
12 Abale okondedwa musadabwe ndi mayesero owawa amene mukukumana nawo ngati kuti china chake chachilendo chakuchitikirani.
Anan su nayi ning, na iwa yene imon fiuwari imusun nle uniu ukan ghe na udi kiti mine bara udumun minuari nafo imomon inanzaghari na se minu.
13 Koma kondwerani popeza mukumva zowawa pamodzi ndi Khristu, kuti mudzakondwere kwakukulu pamene ulemerero wake udzaonekera.
Nafo na ligan gbardang in yinnu nniu in Kristife di, su liburi libo, bara inan su liburi libo nin nayi abo nan nya in yenu ngongong me.
14 Ngati akuchitani chipongwe chifukwa cha dzina la Khristu, ndinu odala, ndiye kuti Mzimu waulemerero wa Mulungu uli pa inu.
Asa izogo fi bara lissan Kristi, udi nin mari, bara Uruhu ngogong nin Nruhu Kutelle sossin litife.
15 Ngati mumva zowawa, zisakhale chifukwa cha kupha munthu, kapena kuba, kapena kuchita choyipa, kapena kulowerera za anthu ena,
Na umong mine nwa neo nafo unan molsu nanit ba.
16 koma ngati mumva zowawa chifukwa ndinu Mkhristu, musachite manyazi, koma muyamike Mulungu chifukwa cha dzinalo.
Vat nani, asa umong mine din niu nafo unan dortu Kutelle, na awa lanza ncin ba, ama na ati Kutelle gongong nan nya lisa me.
17 Pakuti nthawi yafika kuti chiweruzo chiyambe mʼnyumba ya Mulungu, ndipo ngati chiyamba ndi ife nanga podzafika kwa osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu, chidzakhala chotani?
Bara kubi nda na ushara ma cizunu nan nya Kilari Kutelle. Iwa din woru ucizina nin ghiruk, iyaghari ma yitu liyissin na lenge na idi nin yinnu nin liru Kutelle ba?
18 Monga Malemba akuti, “Ngati kuli kovuta kuti olungama apulumuke, nanga munthu wochimwa, wosasamala za Mulungu adzatani?”
Andi fa unan katwa kacine mase utucu bara uniuwari, iyaghari ma yiti liyissin nnan sali fiue Kutelle nin nan kulapi?
19 Nʼchifukwa chake, iwo amene akumva zowawa monga mwa chifuniro cha Mulungu, adzipereke okha mʼmanja mwa Mlengi wawo wokhulupirika ndi kumapitiriza kuchita zabwino.
Bara nani na alenge na idin niu nafo usu Kutelle ni tilai mine kiti nnan makeke ugegeme ai yita non nimon icine.