< 1 Yohane 3 >

1 Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye.
Behold what manner of love the Father hath bestowed upon us, that we should be called children of God l For this cause the world knoweth us not, because it knew him not.
2 Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili.
Beloved, now are we children of God, and it hath not yet been manifested what we shall be. We know that, when it shall be manifested, we shall be like him; because we shall see him as he is.
3 Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
And every one that hath this hope in Him purifieth himself, even as He is pure.
4 Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo.
Whoever committeth sin transgresseth thereby the law; for sin is a transgression of the law.
5 Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo.
And ye know that he was manifested to take away sins; and in him is no sin.
6 Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
Whoever abideth in him sinneth not; whoever sinneth hath not seen him, nor known him.
7 Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama.
My children, let no one deceive you; he that doeth righteousness is righteous, even as he is righteous.
8 Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
He that committeth sin is of the Devil; for the Devil sinneth from the beginning. For this purpose the Son of God was manifested, that he might destroy the works of the Devil.
9 Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu.
Whoever hath been born of God doth not commit sin, because his seed abideth in him; and he cannot sin, because he hath been born of God.
10 Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.
In this are manifest the children of God and the children of the Devil. Whoever doeth not righteousness is not of God, and he that loveth not his brother.
11 Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake.
For this is the message that ye have heard from the beginning, that we should love one another;
12 Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama.
not as Cain was of the Evil One, and slew his brother. And wherefore did he slay him? Because his own works were evil, and his brother's righteous.
13 Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.
Wonder not, brethren, if the world hateth you.
14 Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa.
We know that we have passed out of death into life, because we love the brethren; he that loveth not abideth in death.
15 Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios g166)
Whoever hateth his brother is a murderer; and ye know that no murderer hath everlasting life abiding in him. (aiōnios g166)
16 Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu.
Herein we know love, in that he laid down his life for us; and we ought to lay down our lives for the brethren.
17 Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
But whoever hath this world's goods, and seeth his brother having need, and shutteth up his compassion from him, how dwelleth the love of God in him?
18 Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
My children, let us not love in word, nor in tongue, but in deed and in truth.
19 Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu,
And hereby we know that we are of the truth, and shall assure our hearts before him;
20 nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.
because if our heart condemn us, God is greater than our heart, and knoweth all things.
21 Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu.
Beloved, if our heart condemn us not, we have confidence toward God;
22 Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa.
and whatever we ask, we receive of him, because we keep his commandments, and do the things that are pleasing in his sight.
23 Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira.
And this is his commandment, that we should believe in the name of his Son Jesus Christ, and should love one another, as he gave commandment.
24 Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.
And he that keepeth his commandments abideth in him, and he in him; and hereby we know that he abideth in us, by the Spirit, which he gave us.

< 1 Yohane 3 >