< 1 Akorinto 9 >

1 Kodi sindine mfulu? Kodi sindine mtumwi? Kodi sindinamuone Ambuye athu Yesu? Kodi inu sindiye zotsatira za ntchito yanga mwa Ambuye?
Bhuli, nne nngabha nanngwana? Bhuli, nne nngabha ntume? Bhuli, nne nangaabhona a Yeshu Bhakulungwa bhetu? Bhuli, mmanganya kulundana kwenunji na Bhakulungwa nngabha kwa ligongo lya liengo lyangu?
2 Ngakhale kwa ena sindingakhale mtumwi, mosakayika ndine mtumwi kwa inu! Poti inu ndi chizindikiro cha utumwi wanga mwa Ambuye.
Ibhaga nne nngabha ntume kubhandunji bhana, ikabheje kwenu mmanganya nne ntume. Mmanganya ni ukong'ondelo gwa utume gwangu nkulundana kwenunji na a Kilishitu.
3 Kwa iwo wofuna kundizenga milandu ndimawayankha kuti:
Kwa bhene bhannugulanga bhala shingwiibheleketela ni nnei.
4 Kodi ife tilibe ulamuliro wakudya ndi kumwa?
Bhuli, twangali aki ja pegwa shalya na ya papila kwa liengo lyetu?
5 Kodi ife tilibe ulamuliro wotenga mkazi wokhulupirira nʼkumayenda naye monga amachitira atumwi ena ndi abale awo a Ambuye ndiponso Kefa?
Bhuli, twangali aki ja longana naka jwankongwe Nkilishitu, malinga shibhatendanga mitume bhana, ashaalongo ajabhonji Bhakulungwa na nkali a Kepa?
6 Kodi kapena ine ndekha ndi Barnaba ndiye tikuyenera kugwira ntchito kuti tipeze zotisowa?
Eu bhuli, nne na a Bhanabha ni tupingwa kamula liengo nkwiilolesheya indu yetu?
7 Ndani angagwire ntchito ya usilikali namadzipezera yekha zofunika zonse? Kodi ndani amadzala mpesa koma wosadyako zipatso zake? Ndani amaweta nkhosa koma wosamwako mkaka wake?
Bhuli, linjola gani akwiilipila nnyene nniengo lyakwe? Gani apanda mishabhibhu analye iepo yakwe? Gani ashunga likundi anapapile mabhele ga likundi lyakwe?
8 Kodi moti zimene ndikunenazi ndimaganizo a umunthu chabe? Kodi Malamulo sakunena chimodzimodzinso?
Bhuli, ngunabheleketa genega shigundupe? Bhuli, najalakwe shalia jikalugula nneyo peyo?
9 Popeza analemba mʼMalamulo a Mose kuti, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.” Kodi pamene Mulungu ananena zimenezi ankalabadira za ngʼombe zokha?
Ishijandikwa nshalia ja a Musha, “Nnantabhe kang'wa ng'ombe alikubhata yalya.” Bhuli, penepo a Nnungu gubhabheleketaga ga ng'ombe?
10 Ndithu Iyeyo amanena za ifenso, kodi si choncho? Inde, izi anazilemba chifukwa cha ife, pakuti wolima ndiponso wopuntha, onsewo amagwira ntchito mwachiyembekezo chodzagawana zokololazo.
Bhuli, a Nnungu bhakatuganishiyaga uwe pubhabhelekete nneyo? Elo, genega gashinkujandikwa kwa ligongo lyetu, pabha alima, na auna jula, bhowe bhakwetenje aki ja pata upambi gwa mauno.
11 Ngati tidzala mbewu yauzimu pakati panu, kodi ndi chovuta kwambiri kuti tikolole zosowa zathu kuchokera kwa inu?
Monaga uwe tupandile mmbeju ja muntima munkumbi gwenunji, bhuli, ikabha sha mmbone uwe tupataga indu ya pashilambolyo kopoka kwenu mmanganyanji?
12 Ngati ena ali ndi ufulu wothandizidwa ndi inu, kodi ife sitikuyenera kukhala nawo ufulu ochulukirapo? Koma ife sitinagwiritse ntchito ufulu umenewu. Mʼmalo mwake timangodzichitira chilichonse posafuna kutsekereza ena kumva Uthenga Wabwino wa Khristu.
Ibhaga ashimitume bhananji bhakwetenje aki ja jangutilwa na mmanganyanji, bhuli, uwe twangali aki kupunda bhanganyabho? Ikabheje uwe tushikujileka jene akijo, ikabhe twashinkwiipililila nkupinga tunajibhishile shigwegwe shoshowe Ngani ja Mmbone ja a Kilishitu.
13 Kodi simukudziwa kuti wogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amapeza chakudya chawo mʼNyumbamo, ndipo kuti otumikira pa guwa lansembe amagawana zimene zaperekedwa pa guwa lansembelo.
Mmanganya mmumanyinji kuti, bhaakamulanga liengo nniekalu bhanapatanga yalya nniekalu, na bhatendanga liengo lya bhishila mbepei pa shitala, bhanapatanga lipungu lya mbepeiyo.
14 Chomwechonso Ambuye akulamula kuti wolalikira Uthenga Wabwino azilandira thandizo lawo polalikira Uthenga Wabwinowo.
Nneyo peyo Bhakulungwa bhashiamulisha kuti, bhaalunguyanga Ngani ja Mmbone bhapatanje ya lamila Nngani ja Mmbonemo.
15 Koma ine sindinagwiritse ntchito ufulu woterewu. Sindikulemba izi ndi chiyembekezo choti mundichitire zoterezi. Kuli bwino ndife kusiyana nʼkuti wina alande zomwe ndimazinyadira.
Ikabheje, nne nangalonga yene akiyo wala jimo. Na wala ngajandika gegano nkupinga mbate yene akiyo, pabha kwangu nne, mbaya niiwile ikabheje nngabha mundu amone kuti ngunakwiiniya payoyo.
16 Komatu ndikamalalikira Uthenga Wabwino, sindingadzitamandire popeza ndimawumirizidwa kulalikira. Tsoka kwa ine ngati sindilalikira Uthenga Wabwino!
Ibhaga ngulunguya Ngani ja Mmbone, lyenelyo nngabha lya kwiipunila, pabha njipegwa amuli. Numbe ole gwangu, monaga ngalunguye Ngani ja Mmbone!
17 Ngati ndikugwira ntchitoyi mwakufuna kwanga, ndili ndi mphotho; koma ngati si mwakufuna kwanga, ndiye kuti ntchitoyi ndi Ambuye anandipatsa.
Ibhaga ngakamwile lyene liengoli kwa engwa kwangu, bhai ngalolele kulipwa, ikabheje ngaakamula kwa engwa kwangu, ikabhe ngunapinjikwa kukamula lyene liengoli.
18 Tsono mphotho yanga ndi chiyani? Ndi iyi: kuti polalikira Uthenga Wabwino ndiwupereke kwaulere komanso kuti ndisagwiritse ntchito ufulu wanga polalikira uthengawo.
Bhai nshaala gwangu nndi? Nshaala gwangu ni nema ja lunguya Ngani ja Mmbone, gwangali kulonga aki yangu ya nkulunguya.
19 Ngakhale ndine mfulu ndipo sindine kapolo wa munthu, ndimadzisandutsa kapolo wa aliyense kuti ndikope ambiri mmene ndingathere.
Kwa nneyo, nkali nne nili nngabha nantumwa juka mundu jojowe, njikwiitenda nantumwa juka kila mundu, nkupinga naapatanje bhandu bhabhagwinji.
20 Kwa Ayuda ndimakhala ngati Myuda kuti ndikope Ayuda. Kwa olamulidwa ndi Malamulo ndimakhala ngati wolamulidwa nawo (ngakhale kuti sindine wolamulidwa ndi Malamulowo) kuti ndikope amene amalamulidwa ndi Malamulo.
Ku Bhayaudi nashinkutama mbuti Nanyaudi, nkupinga naapatanje Bhayaudi. Nguti, ku bhandu bha shalia, nashinkwiitenda mbuti mundu jwa shalia, nkali nili nngabha mundu jwa shalia, nkupinga naapatanje bhandu bha shalia.
21 Kwa amene alibe Malamulo ndimakhala wopanda Malamulo (ngakhale kuti sindine wopanda Malamulo a Mulungu koma ndili pansi pa ulamuliro wa Khristu) kuti ndikope wopanda Malamulo.
Kubhalinginji na shalia, nashinkutama mbuti nangali shalia, nkupinga naapatanje bhangalinginji na shalia. Nngabha kuti nangali shalia ja a Nnungu, ikabhe ngwete shalia ja a Kilishitu.
22 Kwa ofowoka ndimakhala wofowoka, kuti ndikope ofowoka. Ndimachita zinthu zilizonse kwa anthu onse kuti mwanjira ina iliyonse ndipulumutse ena.
Ku bhangalinginji mashili nngulupai, nashinkwiitenda mbuti nangali mashili, nkupinga naapatanje bhangalinginji mashilibho. Nashinkwiitenda kila shindu kubhowe, nkupinga kila mushiibhele, naatapulanje bhananji, munkumbi gwabhonji.
23 Ndimachita zonsezi chifukwa cha Uthenga Wabwino, kuti ndigawane nawo madalitso ake.
Ngunatenda yowei ga ligongo lya Ngani ja Mmbone, nkupinga mbate mboka yakwe.
24 Kodi simukudziwa kuti pa mpikisano wa liwiro onse amathamanga ndithu, koma mmodzi yekha ndiye amalandira mphotho? Motero thamangani kuti mupate mphotho.
Bhuli, nkakumumanyanga kuti pa lubhanja lwa ing'ando, bhowe bhanabhutukanga lubhilo, ikabheje apata upo jumope? Mmutukanje nneyo nkupinga mpatanje upo.
25 Aliyense wochita mpikisano amakonzekera mwamphamvu. Amachita izi kuti alandire mphotho yankhata yamaluwa yomwe imafota. Koma ife timachita izi kuti tilandire mphotho yosafota.
Na kila abhutuka lubhilo, anakwiobhelesheya nileka yowe, bhanatendanga nneyo nkupinga bhapatanje shilemba shiangabhanika, ikabhe uwe tupate shilemba shangaangabhanika.
26 Choncho sindithamanga monga wothamanga wopanda cholinga; komanso sindichita mpikisano wankhonya monga munthu amene amangomenya mophonya.
Nneyo peyo numbe nne ngunabhutuka lubhilo, nkupinga ngombole, ngunakoma ubha nngabha mbuti akoma ubha pangali shindu.
27 Ine ndimazunza thupi langa ndi kulisandutsa kapolo kuti nditatha kulalikira ena, ineyo ndingadzapezeke wosayenera kulandira nawo mphotho.
Ikabhe ngunakushiobhelesheya shiilu shangu ya ukomu, inabhe naalungushiyangaga bhananji, namwene nikanwa.

< 1 Akorinto 9 >