< 1 Mbiri 15 >

1 Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
و داود در شهر خود خانه ها بنا کرد و مکاني براي تابوت خدا فراهم ساخته، خيمه اي به جهت آن برپا نمود.۱
2 Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
آنگاه داود فرمود که غير از لاويان کسي تابوت خدا را برندارد زيرا خداوند ايشان را برگزيده بود تا تابوت خدا بردارند و او را هميشه خدمت نمايند.۲
3 Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
و داود تمامي اسرائيل را در اورشليم جمع کرد تا تابوت خداوند را به مکاني که برايش مهيا ساخته بود، بياورند.۳
4 Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
و داود پسران هارون و لاويان را جمع کرد.۴
5 kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
از بني قَهات اُوريئيلِ رئيس وصد بيست نفر برادرانش را.۵
6 Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
از بني مَراري، عَساياي رئيس ودوست بيست نفر برادرانش را.۶
7 kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
از بني جَرشُوم، يوئيل رئيس و صد وسي نفر برادرانش را.۷
8 kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
از بني اليصافان، شَمَعياي رئيس و دوست نفر برادرانش را.۸
9 kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
از بني حَبرُون، اِيلِيئيل رئيس و هشتاد نفر برادرانش را.۹
10 kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
از بني عُزّيئيل، عَمِّيناداب رئيس وصد و دوازده نفر برادرانش را.۱۰
11 Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
و داود صادوق و ابياتارِکَهَنَه و لاويان يعني اُرِيئيل و عَسايا و يوئيل و شَمَعيا و اِيليئيل و عَمِّيناداب را خوانده،۱۱
12 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
به ايشان گفت: «شما رؤساي خاندانهاي آباي لاويان هستيد؛ پس شما و برادران شما خويشتن را تقديس نماييد تا تابوت يهُوَه خداي اسرائيل را به مکاني که برايش مهيا ساخته ام بياوريد.۱۲
13 Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
زيرا از اين سبب که شما دفعه اول آن را نياورديد، يهُوَه خداي ما بر ما رخنه کرد، چونکه او را بر حسب قانون نطلبيديم.»۱۳
14 Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
پس کاهنان و لاويان خويشتن را تقديس نمودند تا تابوت يهُوَه خداي اسرائيل را بياورند.۱۴
15 Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
و پسران لاويان بر وفق آنچه موسي بر حسب کلام خداوند امر فرموده بود، چوب دستيهاي تابوت خدا را بر کتفهاي خود گذاشته، آن را برداشتند.۱۵
16 Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
و داود رؤساي لاويان را فرمود تا برادران خود مغنيان را با آلات موسيقي از عودها و بربطها سنجها تعين نمايند، تا به آواز بلند و شادماني صدا زنند.۱۶
17 Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
پس لاويان هِيمان بن يوئيل و از برادران او آساف بن بَرَکيا و از برادران ايشان بني مَراري ايتان بن قُوشيا را تعيين نمودند.۱۷
18 ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
و با ايشان از برادران درجه دوم خود: زکريا و بَين و يعريئيل شَميراموت و يحيئيل و عُنِّي و اَلِيآب و بنايا و مَعَسيا و مَتِّتيا و اَليفَليا و مَقَنيا و عُوبيد اَدُوم و يعِيئِيل دربانان را.۱۸
19 Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
و از مغنيان: هِيمان و آساف و ايتان را با سنجهاي برنجين تا بنوازند.۱۹
20 Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
و زَکرّيا و عَزِيئيل و شَميراموت و يحيئيل و عُنِّي و اَليآب و مَعَسيا و بنايا را با عودها بر آلاموت.۲۰
21 ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
و مَتَّتيا و اَليفَليا و مَقَنيا و عُوبيد اَدُوم و يعِيئيل و عَزَريا را با بربطهاي بر ثَمانِي تا پيشرَوِي نمايند.۲۱
22 Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
و کَنَنيا رئيس لاويان بر نغمات بود و مغنّيان را تعليم مي داد زيرا که ماهر بود.۲۲
23 Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
و بَرَکيا و اَلقانَه دربانان تابوت بودند.۲۳
24 Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
و شَبَنيا و يوشافاط و نَتَنئيل و عَماساي و زَکريا و بَنايا و اَلَيعَزَر کَهَنَه پيش تابوت خدا کرنا مي نواختند، و عوبيد اَدُوم و يحيي دربانانِ تابوت بودند.۲۴
25 Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
و داود و مشايخ اسرائيل و سرداران هزاره رفتند تا تابوت عهد خداوند را از خانه عوبيد اَدُوم با شادماني بياورند.۲۵
26 Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
و چون خدا لاويان را که تابوت عهد خداوند را برمي داشتند اعانت کرد، ايشان هفت گاو و هفت قوچ ذبح کردند.۲۶
27 Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
و داود و جميع لاوياني که تابوت را برمي داشتند و مغنيان و کَنَنيا که رئيس نغمات مغنيان بود به کتان نازک ملبس بودند، و داود ايفود کتان دربرداشت.۲۷
28 Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
و تمامي اسرائيل تابوت عهد خداوند را به آواز شادماني و آواز بوق و کرّنا و سنج و عود و بربط مي نواختند.۲۸
29 Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.
و چون تابوت عهد خداوند وارد شهر داود مي شد، ميکال دختر شاؤل از پنجره نگريست و داود پادشاه را ديد که رقص و وجد مي نمايد، او را در دل خود خوار شمرد.۲۹

< 1 Mbiri 15 >