< Filimo 1 >
1 Pol, indji u tie ndu Kristi Yesu, ba-mba vayi ma Timoti hi ni Filimon, ikpan mbu ni ikpan tie ndu mbu,
Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.
2 nda hi ni Afia vayi mbu vrenwa, nda hi ni Akipus ikpan u taku mbu, nda hi ni Chochi wa bi rii ni koh mbi.
Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
3 Dun Aliheri he ni yi ni sie rji ni Irji, Itti mbu ni Bachi Yesu Kristi.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
4 Mi zie bre Irji mu. Mi yo yi ni mi bre mu chachu.
Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
5 Mi woh ye nitu son mba yo'shi ni Irji wa bi he niwu nimi Bachi Yesu mba ni wawu bi hu Irji.
Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
6 Mi bre nitu zohn tu-mbi u yo'shi nitu Irji dun vu-kri nitu toh ba kpie bi ndindima wa ahe ni mbu nimi Kristi.
Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
7 U mi ngyri banbran ni vu-suron nitu son kpa mbi, nitu suron bi wa ba hu Irji ba he ngelelen me ni tie me, vayi.
Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
8 Nika, mi he ni gbengblen suron nimi Kristi wa mi ndi dun wu tie kpe wa-abi dun tie,
Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
9 u mi k'ma bre-wu nitu son u Irji - Ime, Pol, chiche ndji, u zizan mi ndji na ba tro me ni Kristi Yesu.
komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
10 Mi miye u, ivre mu Onisimu, ime mi tima ni brusuna.
ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
11 Ana kpa tie meme niwu, ama zizan ahi vren ndindima niwu u ni me ngame.
Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
12 Mi tru'u dun kma ye niwu, a vren u suron mu.
Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
13 Mi na son ndi mini kawu zi ni me, don dun tie nimu ndu u'mbi, ka mi ri he ni loh nitu itre Irji.
Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
14 Mina son ndi mi tie-kpe hama ni kpa nyime me na. Mina son ndi dun tie ume wa ndi a bi'a dun he nitu gbigbi na u ka he ndi wu tie rji nimi suron ndindima.
Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
15 U a rjuto ahi nitu wayi mba ba chu-u rju rji niwu ni vi tsaa ntoh, nitu ani la kma ye nda he niwu ni wawu ntoh. (aiōnios )
Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios )
16 Ana la tie grahn ngana, ani tie bi zan tie u grahn, immri vayi bi son suron mu. Ahi ndji ndindima nda ri nimi suron mu zan, u gra ma niyi ngame, nimi ikpa yi ni nimi Bachi.
Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
17 U toh bi kpa me nji na ikpan tie ndu niyi, kpa-u ngame na wa bi kpa me.
Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
18 To a tie-kpe wa isuron mbi na banwu na u nda kpa ihla ni yi, ko ani hi nge a kpa, bla yo ni tu mu.
Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
19 Ime Pol, mi nha ni'wwo mu: mi hahn yi. Ana ndi bi kma tie ihla ni'wwo mu na.
Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
20 Eih, vayi, tie nimu wayi nimi Bachi; kpa suron mu ku-si nimi Kristi.
Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
21 Gbengble suron nitu wo-ttre mbi, misi nha ye niyi. Mi toh ndi bi tie bran zan ikpe wa mi meyi me.
Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
22 Nimi ntoh ki, bika mlah mitra u bitsri tie ni mi, don mi si yo'shi ndi nitu ibre mbi, ba nji me kma ye ni yi.
Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
23 Epafras, ikpan mu u tie ndu nimi Kristi Yesu, a-ndi dun mi chi yi.
Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
24 U Markus, Aristachus, Demas, u mba Luka, ba kpukpan tie ndu mu.
Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
25 Dun Liheri u Bachi Mbu Yesu Kristi hu ni suron mbi. Amin
Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.